Categories
YOBU

YOBU 23

Yobu abwereza kukana kuti sanachimwe. Mulungu wosadziwika achita chifuniro chake. Kwambiri ochimwa oyenera kulangidwa akhala bwino m’moyo uno

1 Koma Yobu anayankha, nati,

2 Lero lomwe kudandaula kwanga kumawawa;

kulanga kwanga kuposa kubuula kwanga m’kulemera kwake.

3 Ha! Ndikadadziwa kumene ndikampeza Mulungu,

kuti ndifike kumpando wake!

4 Ndikadalongosola mlandu wanga pamaso pake,

ndikadadzaza m’kamwa mwanga ndi matsutsano.

5 Ndikadadziwa mau akadandiyankha ine,

ndikadazindikira chimene akadanena nane.

6 Akadatsutsana nane kodi mwa mphamvu yake yaikulu?

Iai, koma akadanditcherera khutu.

7 Apo woongoka mtima akadatsutsana naye;

ndipo ndikadapulumuka chipulumukire kwa Woweruza wanga.

8 Taonani, ndikanka m’tsogolo, kulibe Iye;

kapena m’mbuyo sindimzindikira;

9 akachita Iye kulamanzere, sindimpenyerera;

akabisala kulamanja, sindimuona.

10 Koma adziwa njira ndilowayi;

atandiyesa ndidzatuluka ngati golide.

11 Phazi langa lagwiratu moponda Iye,

ndasunga njira yake, wosapatukamo.

12 Sindinabwerera kusiya malamulo a pa milomo yake;

ndasungitsa mau a pakamwa pake koposa lamulo langalanga.

13 Koma Iye ndiye wa mtima umodzi, adzambweza ndani?

Ndi ichi chimene moyo wake uchifuna achichita.

14 Pakuti adzachita chondiikidwiratu;

ndipo zambiri zotere zili ndi Iye.

15 Chifukwa chake ndiopsedwa pankhope pake;

ndikalingirira, ndichita mantha ndi Iye.

16 Pakuti Mulungu walefula mtima wanga,

ndi Wamphamvuyonse wandiopsa.

17 Popeza sindinalikhidwa usanafike mdimawo,

ndipo sanandiphimbire nkhope yanga ndi mdima wa bii.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/23-19fdf6c1cbf04aed83d4155c5d4aa7c3.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *