Categories
YOBU

YOBU 25

Bilidadi akuti munthu sayenera kudziyesa wolungama pamaso pa Mulungu

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha, nati,

2 Kulamulira ndi kuopsa kuli ndi Iye;

achita mtendere pa zam’mwamba zake.

3 Ngati awerengedwa makamu ake?

Ndipo ndaniyo, kuunika kwake sikumtulukira?

4 Potero munthu akhala bwanji wolungama kwa Mulungu?

Kapena wobadwa ndi mkazi akhala woyera bwanji?

5 Taonani, ngakhale mwezi ulibe kuwala;

ndi nyenyezi siziyera pamaso pake;

6 kopambana kotani nanga munthu, ndiye mphutsi!

Ndi wobadwa ndi munthu, ndiye nyongolotsi!

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/25-f6bb25ba6efb11ddaf8650d6fe9dea13.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *