Categories
YOBU

YOBU 32

Elihu adzudzula Yobu ndi mabwenzi atatu omwe

1 Pamenepo amuna atatuwa analeka kumyankha Yobu; pakuti anali wolungama pamaso pake pa iye mwini.

2 Ndipo adapsa mtima Elihu mwana wa Barakele wa ku Buzi, wa chibale cha Ramu, adapsa mtima pa Yobu; pakuti anadziyesera yekha wolungama, wosati Mulungu.

3 Adapsa mtima pa mabwenzi ake atatu omwe, pakuti anasowa pomyankha; koma anamtsutsa Yobu kuti ali woipa.

4 Ndipo Elihu analindira kulankhula ndi Yobu, popeza akulu misinkhu ndi iwowa.

5 Koma pakuona Elihu kuti anthu atatuwa anasowa poyankha pakamwa pao anapsa mtima.

6 Ndipo Elihu mwana wa Barakele wa ku Buzi anayankha, nati,

Ine ndine mnyamata, inu ndinu okalamba;

chifukwa chake ndinadziletsa,

ndi kuopa kukuonetsani monga umo ndayesera ine.

7 Ndinati, Amisinkhu anene,

ndi a zaka zochuluka alangize nzeru.

8 Koma m’munthu muli mzimu,

ndi mpweya wa Wamphamvuyonse wawazindikiritsa.

9 Akulu sindiwo eni nzeru,

ndi okalamba sindiwo ozindikira chiweruzo.

10 Chifukwa chake ndinati, Ndimvereni ine,

inenso ndidzaonetsa monga umo ndayesera ine.

11 Taonani, ndinalindira mau anu,

ndinatcherera khutu zifukwa zanu,

pofunafuna inu ponena.

12 Inde ndinasamalira inu;

koma taonani, panalibe womtsutsa Yobu,

kapena wakumbwezera mau pakati pa inu.

13 Msamati, Tapeza nzeru ndife,

Mulungu akhoza kumkhulula, si munthu ai;

14 popeza sanandiponyere ine mau,

sindidzamyankha ndi maneno anu.

15 Asumwa, sayankhanso, Anawathera mau.

16 Kodi ndidzangolindira popeza sanena iwo,

popeza akhala duu osayankhanso?

17 Ndidzayankha inenso mau anga,

ndidzaonetsa inenso za m’mtima mwanga.

18 Pakuti ndadzazidwa ndi mau,

ndi mzimu wa m’kati mwanga undifulumiza.

19 Taonani, m’chifuwa mwanga muli ngati vinyo

wosowa popungulira,

ngati matumba atsopano akuti aphulike.

20 Ndidzanena kuti chifundo chitsike;

ndidzatsegula milomo yanga ndi kuyankha.

21 Ndisati ndisamalire nkhope ya munthu,

kapena kumtchula munthu maina omdyola nao;

22 pakuti sindidziwa kutchula maina osyasyalika;

ndikatero Mlengi wanga adzandichotsa msanga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/32-00656da0cdf0bdca941ec0d2efa0b7e0.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *