Categories
YOBU

YOBU 41

1 Kodi ukhoza kukokaLeviyatanindi mbedza?

Kapena kukanikiza kalandira wake ndi chingwe?

2 Kodi ukhoza kumanga m’mphuno ndi mlulu?

Kapena kuboola nsagwada wake ndi mbedza?

3 Kodi idzachulukitsa mau akukupembedza?

Kapena idzanena nawe mau ofatsa?

4 Kodi idzapangana ndi iwe,

kuti uitenge ikhale kapolo wako wachikhalire?

5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame?

Kapena udzaimangira anamwali ako kuti aiwete?

6 Kodi opangana malonda adzaitsatsa?

Adzaigawana eni malonda?

7 Kodi udzadzaza khungu lake ndi ntchetho,

kapena mutu wake ndi miomba?

8 Isanjike dzanja lako;

ukakumbukira nkhondoyi, sudzateronso.

9 Taona, chiyembekezo chako cha pa iyo chipita pachabe.

Kodi sadzatenga nkhawa munthu pakungoiona?

10 Palibe wolimba mtima kuti adzaiputa.

Ndipo ndaniyo adzaima pamaso pa Ine?

11 Ndaniyo anayamba kundipatsa Ine kuti ndimthokoze?

Zilizonse pansi pa thambo ponse ndi zanga.

12 Sindikhala chete osatchula ziwalo za ng’onayo,

ndi mbiri ya mphamvu yake, ndi makonzedwe ake okoma.

13 Ndani adzasenda chovala chake chakunja?

Adzalowa ndani kumizere iwiri ya mano ake?

14 Adzatsegula ndani zitseko za pakamwa pake?

Mano ake aopsa pozungulira pao.

15 Mamba ake olimba ndiwo kudzitama kwake;

amangika pamodzi ngati okomeredwatu.

16 Alumikizana lina ndi linzake,

mphepo yosalowa pakati pao.

17 Amamatirana lina ndi linzake,

agwirana osagawanikana.

18 Pakuyetsemula ing’anipitsa kuunika,

ndi maso ake akunga zikope za m’mawa.

19 M’kamwa mwake mutuluka miuni,

mbaliwali za moto zibukamo.

20 M’mphuno mwake mutuluka utsi,

ngati nkhali yobwadamuka ndi moto wa zinyatsi

21 mpweya wake uyatsa makala,

ndi m’kamwa mwake mutuluka lawi la moto.

22 Kukhosi kwake kukhala mphamvu,

ndi mantha avumbuluka patsogolo pake.

23 Nyama yake yopsapsala igwirana

ikwima pathupi pake yosagwedezeka.

24 Mtima wake ulimba ngati mwala,

inde ulimba ngati mwala wa mphero.

25 Ikanyamuka, amphamvu achita mantha;

chifukwa cha kuopsedwa azimidwa nzeru.

26 Munthu akaiyamba ndi lupanga, ligoma;

ngakhale nthungo, kapena muvi, kapena mkondo.

27 Chitsulo ichiyesa phesi,

ndi mkuwa ngati mtengo woola.

28 Muvi suithawitsa,

miyala ya pachoponyera iisandutsa chiputu.

29 Zibonga ziyesedwa chiputu,

iseka kuthikuza kwake kwa nthungo.

30 Kumimba kwake ikunga mapale akuthwa,

itasalala kuthope ngati chopunthira.

31 Ichititsa nthubwinthubwi pozama ngati nkhali,

isanduliza nyanja ikunge mafuta.

32 Ichititsa mifunde yonyezimira pambuyo pake;

munthu akadati pozama pali ndi imvi.

33 Padziko lapansi palibe china cholingana nayo,

cholengedwa chopanda mantha.

34 Ipenya chilichonse chodzikuza,

ndiyo mfumu ya zodzitama zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/41-f9fb380fe6f436d6af11a46c49efd6ed.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *