Categories
MASALIMO

MASALIMO Mau Oyamba

Mau Oyamba

Ili ndi buku la nyimbo ndi mapemphero. Mau ake adalembedwa ndi anthu osiyanasiyana pa nthawi yaitali, ndipo Aisraele ankagwiritsa ntchito mauwo popembedza Yehova. Masalimowo alipo amitundumitundu: ena ndi nyimbo zotamanda Mulungu, zopembedza, kapena zothokoza; ena ndi mau opempha chithandizo ndi chitetezo pa nthawi ya mavuto, ena ndi mau olapa ndi opepesera machimo, mau opempha chikhululukiro, mwinanso mau opempha Mulungu kuti alange adani. Masalimowo ngothandiza anthu pakupemphera, aliyense molingana ndi zimene zadzaza mumtima wake, komanso moganizira zosowa za anthu onse a Mulungu ndi ubwino wao. Yesu nayenso ankagwiritsa ntchito Masalimowo popemphera; ndipo kuyambira pa chiyambi cha Mpingo, Akhristu akhala akugwiritsa ntchito buku lomwelo pamwambo wachipembedzo.

Za mkatimu

Bukuli lili ndi zigawo zisanu:

Masalimo 1 mpaka 41

Masalimo 42 mpaka 72

Masalimo 73 mpaka 89

Masalimo 90 mpaka 106

Masalimo 107 mpaka 150

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *