Categories
MASALIMO

MASALIMO 2

Ufumu wa wodzozedwa wa Yehova

1 Aphokoseranjiamitundu,

nalingiriranji anthu zopanda pake?

2 Adzikhazikitsa mafumu a dziko lapansi,

nachita upo akulu pamodzi,

Kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, ndi kuti,

3 Tidule zomangira zao,

titaye nsinga zao.

4 Wokhala m’mwambayo adzaseka;

Ambuye adzawanyoza.

5 Pomwepo adzalankhula nao mu mkwiyo wake,

nadzawaopsa mu ukali wake.

6 Koma Ine ndadzoza mfumu yanga

PaZiyoni, phiri langa loyera.

7 Ndidzauza za chitsimikizo:

Yehova ananena ndi Ine,

Iwe ndiwe Mwana wanga; Ine lero ndakubala.

8 Undifunse, ndipo ndidzakupatsa amitundu

akhale cholowa chako,

ndi malekezero a dziko lapansi akhale akoako.

9 Udzawathyola ndi ndodo yachitsulo;

udzawaphwanya monga mbiya ya woumba.

10 Tsono, mafumu inu, chitani mwanzeru;

langikani, oweruza inu a dziko lapansi.

11 Tumikirani Yehova ndi mantha,

ndipo kondwerani ndi chinthenthe.

12 Mpsompsoneni Mwanayo, kuti angakwiye,

ndipo mungatayike m’njira

ukayaka pang’ono pokha mkwiyo wake.

Odala onse akumkhulupirira Iye.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/2-0cb4e5951d6c2f03d6a79956f669cf45.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *