Categories
MASALIMO

MASALIMO 3

Kukhulupirika kwa Mulungu

Salimo la Davide, muja anathawa Abisalomu mwana wake.

1 Yehova! Ha! Achuluka nanga akundisautsa ine!

Akundiukira ine ndi ambiri.

2 Ambiri amati kwa moyo wanga,

alibe chipulumutso mwa Mulungu.

3 Ndipo Inu Yehova, ndinu chikopa changa;

ulemerero wanga, ndi wondiweramutsa mutu wanga.

4 Ndifuula kwa Yehova ndi mau anga,

ndipo andiyankha m’phiri lake loyera.

5 Ndinagona ine pansi, ndinagona tulo;

ndinauka; pakuti Yehova anandichirikiza.

6 Sindidzaopa unyinji wa anthu akundizinga ine.

7 Ukani Yehova; ndipulumutseni, Mulungu wanga!

Pakuti mwapanda adani anga onse patsaya;

mwawathyola mano oipawo.

8 Chipulumutso ncha Yehova;

dalitso lanu likhale pa anthu anu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/3-60f1eca1f3eec23e92384018de71d6bc.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *