Categories
MASALIMO

MASALIMO 4

Pemphero posautsidwa

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Salimo la Davide.

1 Pakufuula ine mundiyankhe, Mulungu wa chilungamo changa;

pondichepera mwandikulitsira malo.

Ndichitireni chifundo, imvani pemphero langa.

2 Amuna inu, ulemu wanga udzakhala wamanyazi kufikira liti?

Mudzakonda zachabe, ndi kufunafuna bodza kufikira liti?

3 Koma dziwani kuti Yehova anadzipatulira yekha womkondayo,

adzamva Yehova m’mene ndimfuulira Iye.

4 Chitani chinthenthe, ndipo musachimwe.

Nenani mumtima mwanu pakama panu, ndipo mukhale chete.

5 Iphani nsembe za chilungamo,

ndipo mumkhulupirire Yehova.

6 Ambiri amati, Adzationetsa chabwino ndani?

Weramutsirani ife kuunika kwa nkhope yanu, Yehova.

7 Mwapatsa chimwemwe mumtima mwanga,

chakuposa chao m’nyengo yakuchuluka dzinthu zao ndi vinyo wao.

8 Ndi mtendere ndidzagona pansi, pomwepo ndidzagona tulo;

chifukwa Inu, Yehova, mundikhalitsa ine, ndikhale bwino.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/4-41ebdc08e25d9ab62ee6ed79d53b14ad.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *