Categories
MASALIMO

MASALIMO 5

Matsoka a oipa, madalitso a olungama

Kwa Mkulu wa Nyimbo: aimbire zitoliro. Salimo la Davide.

1 Mverani mau anga, Yehova, Zindikirani kulingirira kwanga.

2 Tamvetsani mau a kufuula kwanga,

Mfumu yanga, ndi Mulungu wanga;

pakuti kwa Inu ndimapemphera.

3 M’mawa, Yehova, mudzamva mau anga;

m’mawa, ndidzakukonzerani pemphero langa, ndipo ndidzadikira.

4 Pakuti Inu sindinu Mulungu wakukondwera nacho choipa

mphulupulu siikhala ndi Inu.

5 Opusa sadzakhazikika pamaso panu,

mudana nao onse akuchita zopanda pake.

6 Mudzaononga iwo akunena bodza;

munthu wokhetsa mwazi ndi wachinyengo,

Yehova anyansidwa naye.

7 Koma ine, mwa kuchuluka kwa chifundo chanu

ndidzalowa m’nyumba yanu;

ndidzagwada kuyang’ana Kachisi wanu woyera ndi kuopa Inu.

8 Yehova, munditsogolere m’chilungamo chanu,

chifukwa cha akundizondawo;

mulungamitse njira yanu pamaso panga.

9 Pakuti m’kamwa mwao mulibe mau okhazikika;

m’kati mwao m’mosakaza;

m’mero mwao ndi manda apululu;

lilime lao asyasyalika nalo.

10 Muwayese otsutsika Mulungu;

agwe nao uphungu wao.

M’kuchuluka kwa zolakwa zao muwapirikitse;

pakuti anapikisana ndi Inu.

11 Koma akondwere onse amene athawira kwa Inu,

afuule mokondwera kosaleka, popeza muwafungatira;

nasekere mwa Inu iwo akukonda dzina lanu.

12 Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungamayo;

mudzamtchinjiriza nacho chivomerezo ngati chikopa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/5-7ac8e9291abfdad07ec8a74c1b4764ae.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *