Categories
MASALIMO

MASALIMO 9

Ayamikira chipulumutso chachikulu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Muti-Labeni. Salimo la Davide.

1 Ndidzayamika Yehova ndi mtima wanga wonse;

ndidzawerengera zodabwitsa zanu zonse.

2 Ndidzakondwerera ndi kusekera mwa Inu;

ndidzaimbira dzina lanu, Wam’mwambamwamba Inu.

3 Pobwerera m’mbuyo adani anga,

akhumudwa naonongeka pankhope panu.

4 Pakuti mwandiweruzira mlandu wanga;

mwakhala pa mpando wachifumu, woweruza wolungama.

5 Mwadzudzulaamitundu, mwaononga woipayo,

mwafafaniza dzina lao kunthawi yonka muyaya.

6 Adaniwo atha psiti, apululuka nthawi zonse;

ndipo mizindayo mwaipasula,

chikumbukiro chao pamodzi chatha.

7 Koma Yehova akhala chikhalire,

anakonzeratu mpando wachifumu wake kuti aweruze.

8 Ndipo Iyeyu adzaweruza dziko lapansi m’chilungamo,

nadzaweruza anthu molunjika.

9 Ndipo Yehova adzakhala msanje kwa iye wokhalira mphanthi.

Msanje m’nyengo za nsautso;

10 ndipo iwo akudziwa dzina lanu adzakhulupirira Inu;

pakuti, Inu Yehova, simunawasiye iwo akufuna Inu.

11 Imbirani zoyamika Yehova, wokhala kuZiyoni;

lalikirani mwa anthu ntchito zake.

12 Pakuti Iye wofuna chamwazi awakumbukira;

saiwala kulira kwa ozunzika.

13 Ndichitireni chifundo, Yehova;

penyani kuzunzika kwanga kumene andichitira ondidawo,

inu wondinyamula kundichotsa kuzipata za imfa.

14 Kuti ndibukitse lemekezo lanu lonse;

pa bwalo la mwana wamkazi wa Ziyoni,

ndidzakondwera nacho chipulumutso chanu.

15 Amitundu anagwa m’mbuna imene anaikumba,

lakodwa phazi lao muukonde anautchera.

16 Anadziwika Yehova, anachita kuweruza,

woipayo anakodwa ndi ntchito ya manja ake.

17 Oipawo adzabwerera kumanda,

inde amitundu onse akuiwala Mulungu.

18 Pakuti sadzaiwalika nthawi zonse waumphawi,

kapena chiyembekezo cha ozunzika sichidzaonongeka kosatha.

19 Ukani, Yehova, asalimbike munthu;

amitundu aweruzidwe pankhope panu.

20 Muwachititse mantha, Yehova;

adziwe amitundu kuti ali anthu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/9-fffea0a1edf8ea5da8db738c323b4b66.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *