Categories
MASALIMO

MASALIMO 20

Kupempherera mfumu potulukira iye kunkhondo

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Yehova akuvomereze tsiku la nsautso;

dzina la Mulungu wa Yakobo likuike pamsanje;

2 likutumizire thandizo lotuluka m’malo oyera,

ndipo likugwirizize kuchokera muZiyoni;

3 likumbukire zopereka zako zonse,

lilandire nsembe yako yopsereza;

4 likupatse cha mtima wako,

ndipo likwaniritse upo wako wonse.

5 Tidzafuula mokondwera mwa chipulumutso chanu,

ndipo m’dzina la Mulungu wathu tidzakweza mbendera;

Yehova akwaniritse mapempho ako onse.

6 Tsopano ndidziwa kuti Yehova apulumutsa wodzozedwa wake;

adzamvomereza mu Mwamba mwake moyera

ndi mphamvu ya chipulumutso cha dzanja lake lamanja.

7 Ena atama magaleta, ndi ena akavalo;

koma ife tidzatchula dzina la Yehova Mulungu wathu.

8 Iwowa anagonjeka, nagwa;

koma ife tauka, ndipo takhala chilili.

9 Yehova, pulumutsani,

mfumuyo ativomereze tsiku lakuitana ife.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/20-17416fa199165412977454d9dde10c18.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *