Categories
2 TIMOTEO

2 TIMOTEO 4

1 Ndikuchitira umboni pamaso pa Mulungu ndiKhristuYesu, amene adzaweruza amoyo ndi akufa, ndi pa maonekedwe ake ndi ufumu wake;

2 lalikira mau; chita nao pa nthawi yake, popanda nthawi yake; tsutsa, dzudzula, chenjeza, ndi kuleza mtima konse ndi chiphunzitso.

3 Pakuti idzafika nthawi imene sadzalola chiphunzitso cholamitsa; komatu poyabwa m’khutu adzadziunjikitsa aphunzitsi monga mwa zilakolako za iwo okha:

4 ndipo adzalubza dala pachoonadi, nadzapatukira kutsata nthano zachabe.

5 Koma iwe, khala maso m’zonse, imva zowawa, chita ntchito ya mlaliki wa Uthenga Wabwino, kwaniritsa utumiki wako.

Paulo azindikira kuti imfa yake mpafupi. Aitana Timoteo amzonde. Mbiri ya Dema ndi ena

6 Pakuti ndilimkuthiridwa nsembe tsopano, ndipo nthawi ya kumasuka kwanga yafika.

7 Ndalimbana nako kulimbana kwabwino, ndatsiriza njirayo, ndasunga chikhulupiriro:

8 chotsalira wandiikira ine korona wa chilungamo, amene Ambuye, woweruza wolungama, adzandipatsa ine tsiku lijalo: ndipo si kwa ine ndekha, komatunso kwa onse amene anakonda maonekedwe ake.

9 Tayesetsa kudza kwa ine msanga:

10 pakuti Dema wandisiya ine, atakonda dziko lino lapansi, napita ku Tesalonika; Kresike ku Galatiya, Tito ku Dalamatiya.

11 Luka yekha ali pamodzi ndi ine. Umtenge Marko, adze pamodzi ndi iwe; pakuti ayenera kunditumikira.

12 Koma Tikiko ndamtuma ku Efeso.

13 Chofunda chija ndinachisiya ku Troasi kwa Karpo, udze nacho pakudza iwe, ndi mabuku, makamaka zikopa zija zolembedwa.

14 Aleksandro wosula mkuwa anandichitira zoipa zambiri: adzambwezera iye Ambuye monga mwa ntchito zake;

15 ameneyo iwenso uchenjere naye; pakuti anatsutsana nao mau athu.

16 Pa chodzikanira changa choyamba panalibe mmodzi anandithangata, koma onse anandisiya; chimenecho chisawerengedwe chowatsutsa.

17 Koma Ambuye anaima nane nandipatsa mphamvu; kuti mwa ine chilalikiro chimveke konsekonse, ndiamitunduonse amve; ndipo ndinalanditsidwa m’kamwa mwa mkango.

18 Ambuye adzandilanditsa ku ntchito yonse yoipa, nadzandipulumutsa ine kulowa Ufumu wake wa Kumwamba; kwa Iye ukhale ulemerero kunthawi za nthawi.Amen.

19 Pereka moni kwa Prisika ndi Akwila, ndi banja la Onesifore.

20 Erasto anakhalira mu Korinto; koma Trofimo ndamsiya wodwala ku Mileto.

21 Tayesetsa kudza isanadze nyengo yachisanu. Akukupatsa moni Yubulo, ndi Pude, ndi Lino, ndi Klaudia, ndi abale onse.

22 Ambuye akhale ndi mzimu wako. Chisomo chikhale nanu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/2TI/4-be63e4433deaf08f0df54ae0ced4d8e1.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *