Amwai amene Yehova akhala Mbusa wao
Salimo la Davide.
1 Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.
2 Andigonetsa kubusa lamsipu,
anditsogolera kumadzi odikha.
3 Atsitsimutsa moyo wanga;
anditsogolera m’mabande a chilungamo, chifukwa cha dzina lake.
4 Inde, ndingakhale ndiyenda m’chigwa cha mthunzi wa imfa,
sindidzaopa choipa; pakuti Inu muli ndi ine;
chibonga chanu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine.
5 Mundiyalikira gome pamaso panga m’kuona kwa adani anga;
mwandidzoza mutu wanga mafuta; chikho changa chisefuka.
6 Inde ukoma ndi chifundo zidzanditsata
masiku onse a moyo wanga,
ndipo ndidzakhala m’nyumba ya Yehova masiku onse.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/23-87d6e75eac2f73168f547c4625dcb6ed.mp3?version_id=1068—