Categories
MASALIMO

MASALIMO 23

Amwai amene Yehova akhala Mbusa wao

Salimo la Davide.

1 Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.

2 Andigonetsa kubusa lamsipu,

anditsogolera kumadzi odikha.

3 Atsitsimutsa moyo wanga;

anditsogolera m’mabande a chilungamo, chifukwa cha dzina lake.

4 Inde, ndingakhale ndiyenda m’chigwa cha mthunzi wa imfa,

sindidzaopa choipa; pakuti Inu muli ndi ine;

chibonga chanu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine.

5 Mundiyalikira gome pamaso panga m’kuona kwa adani anga;

mwandidzoza mutu wanga mafuta; chikho changa chisefuka.

6 Inde ukoma ndi chifundo zidzanditsata

masiku onse a moyo wanga,

ndipo ndidzakhala m’nyumba ya Yehova masiku onse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/23-87d6e75eac2f73168f547c4625dcb6ed.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *