Categories
MASALIMO

MASALIMO 28

Apempha chipulumutso, ayamika populumutsidwa

Salimo la Davide.

1 Kwa Inu, Yehova, ndidzafuulira;

thanthwe langa, musandikhalire ngati wosamva;

pakuti ngati munditontholera ine,

ndidzafanana nao iwo akutsikira kumanda.

2 Mverani mau a kupemba kwanga, pamene ndilirira Inu,

pamene ndikweza manja anga kuloza ponenera panu poyera.

3 Musandikoke kundichotsa pamodzi ndi oipa,

ndi ochita zopanda pake;

amene alankhula zamtendere ndi anansi ao,

koma mumtima mwao muli choipa.

4 Muwapatse monga mwa ntchito zao,

ndi monga mwa choipa chochita iwo;

muwapatse monga mwa machitidwe a manja ao;

muwabwezere zoyenera iwo.

5 Pakuti sasamala ntchito za Yehova,

kapena machitidwe a manja ake,

adzawapasula, osawamanganso.

6 Wodalitsika Yehova, Pakuti adamva mau a kupemba kwanga.

7 Yehova ndiye mphamvu yanga, ndi chikopa changa;

mtima wanga wakhulupirira Iye, ndipo anandithandiza,

chifukwa chake mtima wanga ukondwera kwakukulu;

ndipo ndidzamyamika nayo nyimbo yanga.

8 Yehova ndiye mphamvu yao,

inde mphamvu ya chipulumutso cha wodzozedwa wake.

9 Pulumutsani anthu anu, ndi kudalitsa cholowa chanu;

muwawetenso, ndi kuwanyamula nthawi zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/28-18f7c07f0c5a257e43abf9589f958ea2.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *