Categories
MASALIMO

MASALIMO 30

Mkwiyo wa Mulungu ukhala kanthawi, kuyanja kwao ndi kosatha

Salimo la Davide. Nyimbo yakuperekera nyumba kwa Mulungu.

1 Ndidzakukwezani, Yehova; pakuti mwandinyamutsa,

ndipo simunandikondwetsere adani anga.

2 Yehova, Mulungu wanga,

ndinafuulira kwa Inu, ndipo munandichiritsa.

3 Yehova munabweza moyo wanga kumanda,

munandisunga ndi moyo, kuti ndingatsikire kudzenje.

4 Imbirani Yehova, inu okondedwa ake,

ndipo yamikani pokumbukira chiyero chake.

5 Pakuti mkwiyo wake ukhala kanthawi kokha;

koma kuyanja kwake moyo wonse.

Kulira kuchezera,

koma mamawa kuli kufuula kokondwera.

6 Ndipo ine, ndinanena m’phindu langa,

sindidzagwedezeka nthawi zonse.

7 Inu, Yehova, munakhazikitsa phiri langa ndi kuyanja kwanu;

munabisa nkhope yanu; ndinaopa.

8 Ndinafuulira kwa Inu, Yehova;

kwa Ambuye ndinapemba,

9 M’mwazi mwanga muli phindu lanji,

potsikira ine kudzenje?

Ngati fumbi lidzayamika Inu?

Ngati lidzalalikira choonadi chanu?

10 Mverani, Yehova, ndipo ndichitireni chifundo,

Yehova, mundithandize ndi Inu.

11 Munasanduliza kulira kwanga kukhale kusekera;

munandivula chiguduli changa, ndipo munandiveka chikondwero,

12 kuti ulemu wanga uimbire Inu, wosakhala chete.

Yehova Mulungu wanga, ndidzakuyamikani nthawi zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/30-94c410991fb6fa5a91232c2b3b49d4ac.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *