Categories
TITO

TITO Mau Oyamba

Mau Oyamba

Tito sanali Myuda koma wa mitundu ina. Atatembenuka ndi kulowa mu mpingo, adasanduka mnzake wa Paulo womthandiza pa ntchito yolalikira, namuperekeza pa maulendo ake. Paulo adamsiya ku chilumba cha Krete kuti aziyang’anira mpingo kumeneko.

Pomulembera kalatayi, Paulo akumukumbutsa za makhalidwe oyenera atsogoleri a mpingo, makamaka ku Krete poti anthuwo mbiri yao sinali yabwino. Kenaka akumufotokozera kuti iye ayenera kuphunzitsira magulu ena a Akhristu: azibambo okalamba, amai okalamba (kuti iwonso aziphunzitsa amai achitsikana), achinyamata ndipo akapolo. Potsiriza Paulo alangiza Tito pa za mayendedwe a Chikhristu, kuti adziwe kuyanjanitsa anthu ndi kukopa mitima yao, apewe zilizonse zimene zingabweretse kukangana kapena kupatukana mu mpingo.

Za mkatimu

Mau oyamba 1.1-4

Za atsogoleri a mpingo 1.5-16

Ntchito yosamalira magulu osiyanasiyana mu mpingo 2.1-15

Malangizo ndi mau ena ochenjeza 3.1-11

Mau omaliza 3.12-15

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *