Mwai wa munthu amene Mulungu wamkhululukira
Salimo la Davide. Chilangizo.
1 Wodala munthuyo wokhululukidwa tchimo lake;
wokwiriridwa choipa chake.
2 Wodala munthuyu Yehova samwerengera mphulupulu zake;
ndimo mumzimu mwake mulibe chinyengo.
3 Pamene ndinakhala chete mafupa anga anakalamba
ndi kubuula kwanga tsiku lonse.
4 Chifukwa usana ndi usiku dzanja lanu linandilemera ine;
uwisi wanga unasandulika kuuma kwa malimwe.
5 Ndinavomera choipa changa kwa Inu;
ndipo mphulupulu yanga sindinaibise.
Ndinati, Ndidzaululira Yehova machimo anga;
ndipo munakhululukira choipa cha kulakwa kwanga.
6 Chifukwa chake oyera mtima onse apemphere kwa Inu,
pa nthawi ya kupeza Inu;
indetu pakusefuka madzi aakulu
sadzamfikira iye.
7 Inu ndinu mobisalira mwanga;
m’nsautso mudzandisunga;
mudzandizinga ndi nyimbo za chipulumutso.
8 Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo;
ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang’ana iwe.
9 Musakhale monga kavalo, kapena ngati bulu, wopanda nzeru;
zomangira zao ndizo cham’kamwa ndi chapamutu zakuwakokera,
pakuti ukapanda kutero sadzakuyandikiza.
10 Zisoni zambiri zigwera woipa;
koma chifundo chidzamzinga iye wakukhulupirira Yehova.
11 Sekerani mwa Yehova, ndimo kondwerani inu olungama mtima;
ndipo fuulani mokondwera nonsenu oongoka mtima.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/32-8b62cf41b1629155077301dc08c38e74.mp3?version_id=1068—