Categories
MASALIMO

MASALIMO 43

Davide alira akhale ku Kachisi

1 Mundiweruzire, Mulungu, ndipo mundinenere mlandu kwa anthu opanda chifundo.

Mundilanditse kwa munthu wonyenga ndi wosalungama.

2 Pakuti Inu ndinu Mulungu wa mphamvu yanga; mwanditayiranji?

Ndimayenderanji woliralira chifukwa cha kundipsinja mdani?

3 Tumizirani kuunika kwanu ndi choonadi chanu zinditsogolere;

zindifikitse kuphiri lanu loyera,

kumene mukhala Inuko.

4 Kuti ndipite kufikira guwa la nsembe la Mulungu,

kufikira Mulungu wa chimwemwe changa chenicheni,

ndi kuti ndikuyamikeni ndi zeze, Mulungu, Mulungu wanga.

5 Udziweramiranji moyo wanga iwe?

Ndi kuzingwa m’kati mwanga?

Yembekeza Mulungu: pakuti ndidzamyamikanso,

ndiye chipulumutso cha nkhope yanga, ndi Mulungu wanga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/43-8197488d3ef56fba8d833b7567548e6e.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *