Mulungu ndiye pothawirapo anthu ake
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Chilangizo cha kwa ana a Kora. Pa Alamot. Nyimbo.
1 Mulungu ndiye pothawirapo pathu ndi mphamvu yathu,
thandizo lopezekeratu m’masautso.
2 Chifukwa chake sitidzachita mantha,
lingakhale lisandulika dziko lapansi,
angakhale mapiri asunthika, nakhala m’kati mwa nyanja.
3 Chinkana madzi ake akokoma, nachita thovu,
nagwedezeka mapiri ndi kudzala kwake.
4 Pali mtsinje, ngalande zake zidzakondweretsa mzinda wa Mulungu.
Malo oyera okhalamo Wam’mwambamwamba.
5 Mulungu ali m’kati mwake, sudzasunthika,
Mulungu adzauthandiza mbandakucha.
6 Amitunduanapokosera, maufumu anagwedezeka,
ananena mau, dziko lapansi linasungunuka.
7 Yehova wa makamu ali ndi ife;
Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu.
8 Idzani, penyani ntchito za Yehova,
amene achita zopululutsa padziko lapansi.
9 Aletsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi;
athyola uta, nadula nthungo;
atentha magaleta ndi moto.
10 Khalani chete, ndipo dziwani kuti Ine ndine Mulungu,
Ndidzabuka mwa amitundu,
ndidzabuka padziko lapansi.
11 Yehova wa makamu ali ndi ife,
Mulungu wa Yakobo ndiye pamsanje pathu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/46-bca78a4e765d1c318275c4da76140e29.mp3?version_id=1068—