Categories
MASALIMO

MASALIMO 47

Mau a kulemekeza Mulungu mwini dziko lonse lapansi

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la ana a Kora.

1 Ombani m’manja, mitundu yonse ya anthu;

fuulirani kwa Mulungu ndi liu la kuimbitsa.

2 Pakuti Yehova Wam’mwambamwamba ndiye woopsa;

ndiye mfumu yaikulu padziko lonse lapansi.

3 Atigonjetsera anthu,

naikaamitundupansi pa mapazi athu.

4 Atisankhira cholowa chathu,

chokometsetsa cha Yakobo amene anamkonda.

5 Mulungu wakwera ndi mfuu,

Yehova ndi liu la lipenga.

6 Imbirani Mulungu, imbirani;

imbirani mfumu yathu, imbirani.

7 Pakuti Mulungu ndiye mfumu ya dziko lonse lapansi;

imbirani ndi chilangizo.

8 Mulungu ndiye mfumu ya amitundu,

Mulungu akhala pa mpando wachifumu wake woyera.

9 Akulu a anthu asonkhana

akhale anthu a Mulungu wa Abrahamu,

pakuti zikopa za dziko lapansi nza Mulungu;

akwezeka kwakukulu Iyeyo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/47-3f699d23b0b2fdb809c608e8b2a6d8f4.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *