Categories
MASALIMO

MASALIMO 48

Ukoma ndi ulemerero wa Ziyoni

Nyimbo. Salimo la ana a Kora.

1 Yehova ndiye wamkulu, ayenera kulemekezekadi,

m’mzinda wa Mulungu wathu, m’phiri lake loyera.

2 Phiri laZiyoni, chikhalidwe chake nchokoma

kumbali zake za kumpoto,

ndilo chimwemwe cha dziko lonse lapansi,

mzinda wa mfumu yaikulu.

3 Mulungu adziwika m’zinyumba zake ngati msanje.

4 Pakuti, taonani, mafumuwo anasonkhana,

anapitira pamodzi.

5 Anapenya mudziwo, ndipo pamenepo anadabwa;

anaopsedwa, nathawako.

6 Pomwepo anagwidwa nako kunthunthumira;

anamva chowawa, ngati wam’chikuta.

7 Muswa zombo za ku Tarisisi ndi mphepo ya kum’mawa.

8 Monga tidamva, momwemo tidapenya

m’mzinda wa Yehova wa makamu, m’mzinda wa Mulungu wathu,

Mulungu adzaukhazikitsa kunthawi yamuyaya.

9 Tidalingalira zachifundo chanu, Mulungu,

m’kati mwa Kachisi wanu.

10 Monga dzina lanu, Mulungu,

momwemo lemekezo lanu ku malekezero a dziko lapansi;

m’dzanja lamanja lanu mudzala chilungamo.

11 Likondwere phiri la Ziyoni,

asekere ana aakazi a Yuda,

chifukwa cha maweruzo anu.

12 Zungulirani Ziyoni, ndipo muuzinge,

werengani nsanja zake.

13 Penyetsetsani malinga ake,

yesetsani zinyumba zake;

kuti mukaziwerengere mibadwo ikudza m’mbuyo.

14 Pakuti Mulungu ameneyo ndiye Mulungu wathu

kunthawi za nthawi,

adzatitsogolera kufikira imfa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/48-ba5befffea5b0683b72b66ebb5cb961c.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *