Categories
MASALIMO

MASALIMO 60

Madandaulo ndi pempho la Davide

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Susan-Eduti. Mikitamu wa Davide; lakulangiza; muja analimbana nao Aramu Naharaimu ndi Aramu Zoba, nabwera Yowabu anapha a Edomu kuchigwa cha Mchere zikwi khumi mphambu ziwiri.

1 Mwatitaya Mulungu, mwatipasula;

mwakwiya; tibwezereni.

2 Mwagwedeza dziko, mwaling’amba.

Konzani ming’alu yake; pakuti ligwedezeka.

3 Mwaonetsa anthu anu zowawa,

mwatimwetsa vinyo wotinjenjemeretsa.

4 Koma mwapatsa mbendera akuopa Inu,

aikweze chifukwa cha choonadi.

5 Kuti okondedwa anu alanditsidwe,

pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja, ndipo mutivomereze.

6 Mulungu walankhula m’chiyero chake; ndidzakondwerera,

ndidzagawa Sekemu, ndidzayesa muyeso chigwa cha Sukoti.

7 Giliyadi ndi wanga, Manasenso ndi wanga;

ndipo Efuremu ndi mphamvu ya mutu wanga;

Yuda ndiye wolamulira wanga.

8 Mowabu ndiye mkhate wanga;

pa Edomu ndidzaponya nsapato yanga.

Filistiya, fuulatu chifukwa cha ine.

9 Adzandifikitsa ndani m’mzinda wa m’linga?

Adzanditsogolera ndani ku Edomu?

10 Si ndinu, Mulungu, amene mwatitaya?

Osatuluka nao makamu athu, Mulungu.

11 Tithandizeni kunsautso;

kuti chipulumutso cha munthu ndi chabe.

12 Mwa Mulungu tidzachita molimbika mtima,

ndipo Iye adzapondereza otisautsa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/60-396c9720e403cdadaf93d7346d326fac.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *