Poopsedwa Davide athamangira Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Salimo la Davide.
1 Imvani mfuu wanga, Mulungu;
mverani pemphero langa.
2 Ku malekezero a dziko lapansi ndidzafuulira kwa Inu,
pomizika mtima wanga.
Nditsogolereni kuthanthwe londiposa ine m’kutalika kwake.
3 Pakuti munakhala pothawirapo panga;
nsanja yolimba pothawa mdani ine.
4 Ndidzagoneragonerabe m’chihema mwanu;
ndidzathawira mobisalamo m’mapiko anu.
5 Pakuti Inu, Mulungu, mudamva zowinda zanga;
munandipatsa cholowa cha iwo akuopa dzina lanu.
6 Mudzatalikitsa moyo wa mfumu.
Zaka zake zidzafikira mibadwomibadwo.
7 Adzakhala nthawi zonse pamaso pa Mulungu;
mumpatse chifundo ndi choonadi zimsunge.
8 Potero ndidzaimba zolemekeza dzina lanu kunthawi zonse,
kuti ndichite zowinda zanga tsiku ndi tsiku.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/61-1e56a0cd41ef1a4cbbcc64d8486c8292.mp3?version_id=1068—