Mtima woliralira kuyanjana ndi Mulungu
Salimo la Davide; muja anakhala m’chipululu cha Yuda.
1 Inu Mulungu, ndinu Mulungu wanga;
ndidzakufunani m’matanda kucha.
Moyo wanga ukumva ludzu la kwa Inu,
thupi langa lilirira Inu,
m’dziko louma ndi lotopetsa, lopanda madzi.
2 Kuti ndione mphamvu yanu ndi ulemerero wanu,
monga ndinakuonani m’malo oyera.
3 Pakuti chifundo chanu chiposa moyo makomedwe ake;
milomo yanga idzakulemekezani.
4 Potero ndidzakuyamikani m’moyo mwanga;
ndidzakweza manja anga m’dzina lanu.
5 Mudzakhutitsa moyo wanga ngati ndi mafuta ndi zonona;
ndipo pakamwa panga ndidzakulemekezani
ndi milomo yakufuula mokondwera.
6 Pokumbukira Inu pa kama wanga,
ndi kulingalira za Inu maulonda a usiku.
7 Pakuti munakhala mthandizi wanga;
ndipo ndidzafuula mokondwera mu mthunzi wa mapiko anu.
8 Moyo wanga uumirira Inu.
Dzanja lamanja lanu lindigwiriziza.
9 Koma iwo amene afuna moyo wanga kuti auononge,
adzalowa m’munsi mwake mwa dziko.
10 Adzawapereka kumphamvu ya lupanga;
iwo adzakhala gawo la ankhandwe.
11 Koma mfumu idzakondwera mwa Mulungu;
yense wakulumbirira iye adzatamandira;
pakuti pakamwa pa iwo onena bodza padzatsekedwa.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/63-dd5022b579c322c447c9f170e2fa695e.mp3?version_id=1068—