Davide apempha Mulungu amtchinjirize pa omlalira
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.
1 Imvani Mulungu, mau anga, m’kudandaula kwanga;
sungani moyo wanga angandiopse mdani.
2 Ndibiseni pa upo wachinsinsi wa ochita zoipa;
pa phokoso la ochita zopanda pake.
3 Amene anola lilime lao ngati lupanga,
napiringidza mivi yao, ndiyo mau akuwawitsa;
4 kuponyera wangwiro mobisika:
Amponyera modzidzimutsa, osaopa.
5 Alimbikitsana m’chinthu choipa;
apangana za kutchera misampha mobisika;
akuti, Adzaiona ndani?
6 Afunafuna zosalungama; kusanthula, asanthuladi mpaka kutha;
chingakhale cha m’kati mwake mwa munthu, ndi mtima wozama.
7 Koma Mulungu adzawaponyera muvi;
adzalaswa modzidzimutsa.
8 Adzawakhumudwitsa, lilime lao lidzawatsutsa;
onse akuwaona adzawathawa.
9 Ndipo anthu onse adzachita mantha;
nadzabukitsa chochita Mulungu,
nadzasamalira ntchito yake.
10 Wolungama adzakondwera mwa Yehova,
nadzakhulupirira Iye;
ndipo oongoka mtima onse adzalemekeza.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/64-f8cb3fc909cb65eb3e048846840dd693.mp3?version_id=1068—