Davide apempha Mulungu amlanditse msanga
Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide, la chikumbutso.
1 Fulumirani kundipulumutsa, Mulungu!
Fulumirani kundithandiza, Yehova.
2 Achite manyazi, nadodome
amene afuna moyo wanga.
Abwezedwe m’mbuyo, napepulidwe
amene akonda kundichitira choipa.
3 Abwerere, kukhale mphotho ya manyazi ao
amene akuti, Hede, hede.
4 Asekerere nakondwerere mwa Inu onse akufuna Inu;
nanene kosalekeza iwo akukonda chipulumutso chanu,
abuke Mulungu.
5 Koma ine ndine wozunzika ndi waumphawi;
mundifulumirire, Mulungu.
Inu ndinu mthandizi wanga ndi Mpulumutsi wanga;
musachedwe, Yehova.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/70-251047a461c8e820f60f8ead5989c355.mp3?version_id=1068—