Categories
MASALIMO

MASALIMO 76

Ulemerero ndi mphamvu ya Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Neginoto. Salimo la Asafu. Nyimbo.

1 Mulungu adziwika mwa Yuda,

dzina lake limveka mwa Israele.

2 Msasa wake unali mu Salemu,

ndipo pokhala Iye muZiyoni.

3 Pomwepo anathyola mivi ya pauta;

chikopa, ndi lupanga, ndi nkhondo.

4 Inu ndinu wakuunikira, ndi womveka

wakuposa mapiri muli achifwamba.

5 Olimba mtima chifunkhidwa chuma chao, agona tulo tao;

amuna onse amphamvu asowa manja ao.

6 Pa kudzudzula kwanu, Mulungu wa Yakobo,

galeta ndi kavalo yemwe anagwa m’tulo.

7 Inu ndinu woopsa;

ndipo utauka mkwiyo wanu adzakhala chilili ndani pamaso panu?

8 Mudamveketsa chiweruzo chochokera Kumwamba;

dziko lapansi linachita mantha, nilinakhala chete,

9 pakuuka Mulungu kuti aweruze,

kuti apulumutse ofatsa onse a padziko lapansi.

10 Indedi, kuzaza kwake kwa munthu kudzakulemekezani;

chotsalira cha kuzazaku mudzachiletsa.

11 Windani ndipo chitirani Yehova Mulungu wanu zowindazo;

onse akumzinga abwere nacho chopereka

cha kwa Iye amene ayenera kumuopa.

12 Iye adzadula mzimu wa akulu;

akhala woopsa kwa mafumu a padziko lapansi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/76-6d49cd8d3a95a8d09509157e28fcb6e7.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *