Categories
MASALIMO

MASALIMO 82

Oweruza aweruza bwino

Salimo la Asafu.

1 Mulungu aima mu msonkhano wa Mulungu,

aweruza pakati pa milungu.

2 Mudzaweruza mosalunjika kufikira liti,

ndi kusamalira nkhope ya oipa?

3 Weruzani osauka ndi amasiye;

weruzani molungama ozunzika ndi osowa.

4 Pulumutsani osauka ndi aumphawi;

alanditseni m’dzanja la oipa.

5 Sadziwa, ndipo sazindikira;

amayendayenda mumdima;

maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.

6 Ndinati Ine, Inu ndinu milungu,

ndi ana a Wam’mwambamwamba nonsenu.

7 Komatu mudzafa monga anthu,

ndipo mudzagwa monga wina wa akulu.

8 Ukani, Mulungu, weruzani dziko lapansi;

pakuti Inu mudzalandira amitundu onse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/82-51f5963a0b1ec07d9942f2c0062d9534.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *