Oweruza aweruza bwino
Salimo la Asafu.
1 Mulungu aima mu msonkhano wa Mulungu,
aweruza pakati pa milungu.
2 Mudzaweruza mosalunjika kufikira liti,
ndi kusamalira nkhope ya oipa?
3 Weruzani osauka ndi amasiye;
weruzani molungama ozunzika ndi osowa.
4 Pulumutsani osauka ndi aumphawi;
alanditseni m’dzanja la oipa.
5 Sadziwa, ndipo sazindikira;
amayendayenda mumdima;
maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6 Ndinati Ine, Inu ndinu milungu,
ndi ana a Wam’mwambamwamba nonsenu.
7 Komatu mudzafa monga anthu,
ndipo mudzagwa monga wina wa akulu.
8 Ukani, Mulungu, weruzani dziko lapansi;
pakuti Inu mudzalandira amitundu onse.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/82-51f5963a0b1ec07d9942f2c0062d9534.mp3?version_id=1068—