Categories
MASALIMO

MASALIMO 83

Amitundu apangana kuononga Aisraele. Apempha Mulungu awalanditse

Nyimbo. Salimo la Asafu.

1 Mulungu musakhale chete;

musakhale duu, osanena kanthu, Mulungu.

2 Pakuti taonani, adani anu apokosera,

ndipo okwiyira Inu aweramutsa mutu.

3 Apangana mochenjerera pa anthu anu,

nakhalira upo pa obisika anu.

4 Amati, Tiyeni tiwaononge asakhalenso mtundu wa anthu;

ndipo dzina la Israele lisakumbukikenso.

5 Pakuti anakhalira upo ndi mtima umodzi;

anachitachipanganocha pa Inu.

6 Mahema a Edomu ndi a Aismaele;

Mowabu ndi Ahagiri;

7 Gebala ndi Amoni ndi Amaleke;

Filistiya, pamodzi ndi iwo okhala mu Tiro.

8 Asiriya anaphatikana nao;

anakhala dzanja la ana a Loti.

9 Muwachitire monga munachitira Midiyani;

ndi Sisera, ndi Yabini kumtsinje wa Kisoni,

10 amene anaonongeka ku Endori;

anakhala ngati ndowe ya kumunda.

11 Muwaike akulu ao ngati Orebu ndi Zeebu;

mafumu ao ngati Zeba ndi Zalimuna,

12 amene anati, Tilande malo okhalamo Mulungu, akhale athu.

13 Mulungu wanga, muwaike akhale ngati mungu;

ngati ziputu zomka ndi mphepo.

14 Monga moto upsereza nkhalango,

ndi monga lawi liyatsa mapiri.

15 Momwemo muwatsate ndi namondwe,

nimuwaopse ndi kamvulumvulu wanu.

16 Achititseni manyazi pankhope pao;

kuti afune dzina lanu, Yehova.

17 Achite manyazi, naopsedwe kosatha;

ndipo asokonezeke, naonongeke.

18 Kuti adziwe kuti inu nokha, dzina lanu ndinu Yehova,

ndinu Wam’mwambamwamba padziko lonse lapansi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/83-d2cdb0eba6aa3310d96e8863b2c3cdf6.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *