Categories
MASALIMO

MASALIMO 85

Akumbutsa Mulungu madalitso akale, apempha awabwereze

Kwa Mkulu wa Nyimbo: Salimo la ana a Kora.

1 Munachita zovomereza dziko lanu, Yehova;

munabweza ukapolo wa Yakobo.

2 Munachotsa mphulupulu ya anthu anu,

munafotsera zolakwa zao zonse.

3 Munabweza kuzaza kwanu konse;

munabwerera kumkwiyo wanu wotentha.

4 Mutibweze, Mulungu wa chipulumutso chathu,

nimuletse udani wanu wa pa ife.

5 Kodi mudzatikwiyira nthawi zonse?

Kodi mudzakhala chikwiyire mibadwomibadwo?

6 Kodi simudzatipatsanso moyo,

kuti anthu anu akondwerere ndi Inu?

7 Tionetseni chifundo chanu, Yehova,

tipatseni chipulumutso chanu.

8 Ndidzamva cholankhula Mulungu Yehova;

pakuti adzalankhula zamtendere ndi anthu ake,

ndi okondedwa ake;

koma asabwererenso kuchita zopusa.

9 Indedi chipulumutso chake chili pafupi

ndi iwo akumuopa Iye;

kuti m’dziko mwathu mukhale ulemu.

10 Chifundo ndi choonadi zakomanizana;

chilungamo ndi mtendere zapsompsonana.

11 Choonadi chiphukira m’dziko;

ndi chilungamo chasuzumira chili m’mwamba.

12 Inde Yehova adzapereka zokoma;

ndipo dziko lathu lidzapereka zipatso zake.

13 Chilungamo chidzamtsogolera;

ndipo chidzamkonzera mapazi ake njira.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/85-c4c844fc1b8f723f7281b828236e7378.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *