Anthu onse ayamike Mulungu chifukwa cha ntchito zake, chilungamo chake, ndi chifundo chake
Salimo, Nyimbo ya pa Sabata.
1 Nkokoma kuyamika Yehova,
ndi kuimbira nyimbo dzina lanu, Wam’mwambamwamba Inu.
2 Kuonetsera chifundo chanu mamawa,
ndi chikhulupiriko chanu usiku uliwonse.
3 Pa choimbira cha zingwe khumi ndi pachisakasa;
pazeze ndi kulira kwake.
4 Popeza Inu, Yehova, munandikondweretsa ndi kuchita kwanu,
ndidzafuula mokondwera pa ntchito ya manja anu.
5 Ha! Ntchito zanu nzazikulu, Yehova,
zolingalira zanu nzozama ndithu.
6 Munthu wopulukira sachidziwa;
ndi munthu wopusa sachizindikira ichi;
7 chakuti pophuka oipa ngati msipu,
ndi popindula ochita zopanda pake;
chitero kuti adzaonongeke kosatha.
8 Koma Inu, Yehova, muli m’mwamba kunthawi yonse.
9 Pakuti, taonani, adani anu, Yehova,
pakuti, taonani, adani anu adzatayika;
ochita zopanda pake onse adzamwazika.
10 Koma munakweza nyanga yanga ngati ya njati;
anandidzoza mafuta atsopano.
11 Diso langa lapenya chokhumba ine pa iwo ondilalira,
m’makutu mwanga ndamva chokhumba ine
pa iwo akuchita zoipa akundiukira.
12 Wolungama adzaphuka ngati mgwalangwa;
adzakula ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
13 Iwo ookedwa m’nyumba ya Yehova,
adzaphuka m’mabwalo a Mulungu wathu.
14 Atakalamba adzapatsanso zipatso;
adzadzazidwa ndi madzi nadzakhala abiriwiri,
15 kulalikira kuti Yehova ngwolunjika;
Iye ndiye thanthwe langa, ndipo mwa Iye mulibe chosalungama.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/92-932cff6c0bcd754f622cfa753d8f06fc.mp3?version_id=1068—