Ufumu wa Mulungu ndiwo wa ulemerero, mphamvu, ndi chiyero
1 Yehova achita ufumu; wadziveka ndi ukulu;
wadziveka Yehova, wadzimangirira mphamvu m’chuuno;
dziko lomwe lokhalamo anthu likhakizika, silidzagwedezeka.
2 Mpando wachifumu wanu ukhazikika kuyambira kale lija;
Inu ndinu wosayambira ndi kale lomwe.
3 Mitsinje ikweza, Yehova,
mitsinje ikweza mkokomo wao;
mitsinje ikweza mafunde ao.
4 Yehova Wam’mwamba ndiye wamphamvu,
wakuposa mkokomo wa madzi ambiri,
ndi mafunde olimba a nyanja.
5 Mboni zanu zivomerezeka ndithu;
chiyero chiyenera nyumba yanu,
Yehova, kunthawi za muyaya.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/93-31e10020bca2d40d7747c9da21afd644.mp3?version_id=1068—