Categories
MASALIMO

MASALIMO 93

Ufumu wa Mulungu ndiwo wa ulemerero, mphamvu, ndi chiyero

1 Yehova achita ufumu; wadziveka ndi ukulu;

wadziveka Yehova, wadzimangirira mphamvu m’chuuno;

dziko lomwe lokhalamo anthu likhakizika, silidzagwedezeka.

2 Mpando wachifumu wanu ukhazikika kuyambira kale lija;

Inu ndinu wosayambira ndi kale lomwe.

3 Mitsinje ikweza, Yehova,

mitsinje ikweza mkokomo wao;

mitsinje ikweza mafunde ao.

4 Yehova Wam’mwamba ndiye wamphamvu,

wakuposa mkokomo wa madzi ambiri,

ndi mafunde olimba a nyanja.

5 Mboni zanu zivomerezeka ndithu;

chiyero chiyenera nyumba yanu,

Yehova, kunthawi za muyaya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/93-31e10020bca2d40d7747c9da21afd644.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *