Categories
MASALIMO

MASALIMO 96

Onse a pansi pano ndi am’mwamba omwe alemekeze Mulungu

1 Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano;

muimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi.

2 Muimbireni Yehova, lemekezani dzina lake;

lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

3 Fotokozerani ulemerero wake mwaamitundu;

zodabwitsa zake mwa mitundu yonse ya anthu.

4 Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;

ayenera amuope koposa milungu yonse.

5 Pakuti milungu yonse ya mitundu ya anthu ndiyo mafano,

koma Yehova analenga zakumwamba.

6 Pamaso pake pali ulemu ndi ukulu.

M’malo opatulika mwake muli mphamvu ndi zochititsa kaso.

7 Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,

mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu.

8 Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lake;

bwerani nacho chopereka, ndipo fikani kumabwalo ake.

9 Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa,

njenjemerani pamaso pake, inu dziko lonse lapansi.

10 Nenani mwaamitundu, Yehova achita ufumu;

dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke;

adzaweruza mitundu ya anthu molunjika.

11 Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi;

nyanja ibume mwa kudzala kwake.

12 Munda ukondwerere ndi zonse zili m’mwemo;

pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzafuula mokondwera.

13 Pamaso pa Yehova, pakuti akudza;

pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi

Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi chilungamo,

ndi mitundu ya anthu ndi choonadi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/96-3de72cfe218307b222ad2e70bf7c0450.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *