Onse a pansi pano ndi am’mwamba omwe alemekeze Mulungu
1 Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano;
muimbireni Yehova, inu, dziko lonse lapansi.
2 Muimbireni Yehova, lemekezani dzina lake;
lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Fotokozerani ulemerero wake mwaamitundu;
zodabwitsa zake mwa mitundu yonse ya anthu.
4 Pakuti Yehova ndi wamkulu, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;
ayenera amuope koposa milungu yonse.
5 Pakuti milungu yonse ya mitundu ya anthu ndiyo mafano,
koma Yehova analenga zakumwamba.
6 Pamaso pake pali ulemu ndi ukulu.
M’malo opatulika mwake muli mphamvu ndi zochititsa kaso.
7 Mpatseni Yehova, inu, mafuko a mitundu ya anthu,
mpatseni Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 Mpatseni Yehova ulemerero wa dzina lake;
bwerani nacho chopereka, ndipo fikani kumabwalo ake.
9 Gwadirani Yehova moyera ndi mokometsetsa,
njenjemerani pamaso pake, inu dziko lonse lapansi.
10 Nenani mwaamitundu, Yehova achita ufumu;
dziko lokhalamo anthu lomwe likhazikika kuti silingagwedezeke;
adzaweruza mitundu ya anthu molunjika.
11 Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi;
nyanja ibume mwa kudzala kwake.
12 Munda ukondwerere ndi zonse zili m’mwemo;
pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzafuula mokondwera.
13 Pamaso pa Yehova, pakuti akudza;
pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi
Adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi chilungamo,
ndi mitundu ya anthu ndi choonadi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/96-3de72cfe218307b222ad2e70bf7c0450.mp3?version_id=1068—