Categories
MASALIMO

MASALIMO 98

Alemekeze Mulungu pa chifundo ndi choonadi chao

Salimo.

1 Muimbireni Yehova nyimbo yatsopano;

popeza anachita zodabwitsa:

Dzanja lake lamanja, mkono wake woyera,

zinamchitira chipulumutso.

2 Yehova anawadziwitsira chipulumutso chake;

anaonetsera chilungamo chake pamaso pa amitundu.

3 Anakumbukira chifundo chake ndi chikhulupiriko chake

kunyumba ya Israele;

malekezero onse a dziko lapansi

anaona chipulumutso cha Mulungu wathu.

4 Fuulirani kwa Yehova, inu, dziko lonse lapansi;

kuwitsani ndi kufuulira mokondwera;

inde, imbirani zomlemekeza.

5 Muimbireni Yehova zomlemekeza ndi zeze;

ndi zeze ndi mau a salimo.

6 Fuulani pamaso pa Mfumu Yehova,

ndi mbetete ndi liu la lipenga.

7 Nyanja ifuule ndi kudzala kwake;

dziko lokhalamo anthu ndi iwo okhalamo;

8 mitsinje iombe m’manja;

mapiri afuule pamodzi mokondwera.

9 Pamaso pa Yehova, popeza akudza kudzaweruza dziko lapansi;

adzaweruza dziko lokhalamo anthu ndi chilungamo,

ndipo mitundu ya anthu molunjika.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/98-ac8f04ab9533726087f9e969fcb70cf5.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *