Categories
MASALIMO

MASALIMO 102

Wopsinjika apempha Mulungu achitire anthu ake chifundo, amitundu nammverenso

Pemphero la Wozunzika, m’mene anakomoka natsanulira cholingalira chake pamaso pa Yehova.

1 Yehova, imvani pemphero langa,

ndipo mfuu wanga ufikire Inu.

2 Musandibisire nkhope yanu tsiku la nsautso yanga;

munditchereze khutu lanu;

tsiku limene ndiitana ine mundiyankhe msanga.

3 Popeza masiku anga akanganuka ngati utsi,

ndi mafupa anga anyeka ngati nkhuni.

4 Mtima wanga ukunga udzu womweta, nufota;

popeza ndiiwala kudya mkate wanga.

5 Chifukwa cha liu la kubuula kwanga

mnofu wanga umamatika kumafupa anga.

6 Ndikunga vuwo m’chipululu;

ndikhala ngati kadzidzi wa kumabwinja.

7 Ndidikira, ndikhala ngati mbalame

ili yokha pamwamba pa tsindwi.

8 Adani anga anditonza tsiku lonse;

akundiyalukirawo alumbirira ine.

9 Pakuti ndadya mapulusa ngati mkate,

ndi kusakaniza chomwera changa ndi misozi,

10 chifukwa cha ukali wanu ndi kuzaza kwanu;

popeza munandinyamula ndipo munandigwetsa.

11 Masiku anga akunga mthunzi womka m’tali;

ndipo ine ndauma ngati udzu.

12 Koma Inu, Yehova, mukhalabe kunthawi yonse;

ndi chikumbukiro chanu ku mibadwomibadwo.

13 Inu mudzauka, ndi kuchitira nsoniZiyoni;

popeza yafika nyengo yakumchitira chifundo, nyengo yoikika.

14 Pakuti atumiki anu akondwera nayo miyala yake,

nachitira chifundo fumbi lake.

15 Pamenepoamitunduadzaopa dzina la Yehova,

ndi mafumu onse a dziko lapansi ulemerero wanu.

16 Pakuti Yehova anamanga Ziyoni,

anaoneka mu ulemerero wake;

17 anasamalira pemphero la iwo akusowa konse,

osapepula pemphero lao.

18 Ichi adzachilembera mbadwo ukudza;

ndi mtundu wa anthu umene udalengedwa udzamlemekeza Yehova.

19 Pakuti anapenya pansi ali kumwamba kuli malo ake opatulika;

Yehova pokhala kumwamba anapenya dziko lapansi;

20 kuti amve kubuula kwa wandende;

namasule ana a imfa.

21 Kuti anthu alalikire dzina la Yehova mu Ziyoni,

ndi chilemekezo chake muYerusalemu;

22 Posonkhana pamodzi mitundu ya anthu,

ndi maufumu kuti atumikire Yehova.

23 Iye analanda mphamvu yanga panjira;

anachepsa masiku anga.

24 Ndinati, Mulungu wanga, musandichotse pakati pa masiku anga:

Zaka zanu zikhalira m’mibadwomibadwo.

25 Munakhazika dziko lapansi kalelo;

ndipo zakumwamba ndizo ntchito ya manja anu.

26 Zidzatha izi, koma Inu mukhala:

Inde, zidzatha zonse ngati chovala;

mudzazisintha ngati malaya, ndipo zidzasinthika:

27 Koma Inu ndinu yemweyo,

ndi zaka zanu sizifikira kutha.

28 Ana a atumiki anu adzakhalitsa,

ndi mbeu zao zidzakhazikika pamaso panu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/102-49465b440a1a1f3bc67c9b0b36b64c7c.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *