Categories
MASALIMO

MASALIMO 121

Mulungu Msungi wokhulupirika wa anthu ake

Nyimbo yokwerera.

1 Ndikweza maso anga kumapiri:

Thandizo langa lidzera kuti?

2 Thandizo langa lidzera kwa Yehova,

wakulenga kumwamba ndi dziko lapansi.

3 Sadzalola phazi lako literereke:

Iye amene akusunga sadzaodzera.

4 Taonani, wakusunga Israele

sadzaodzera kapena kugona.

5 Yehova ndiye wakukusunga;

Yehova ndiye mthunzi wako wa kudzanja lako lamanja.

6 Dzuwa silidzawamba usana,

mwezi sudzakupanda usiku.

7 Yehova adzakusunga kukuchotsera zoipa zilizonse;

adzasunga moyo wako.

8 Yehova adzasungira kutuluka kwako ndi kulowa kwako,

kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/121-fa95c6d1f2abdc05f916ba5667688051.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *