Categories
MASALIMO

MASALIMO 125

Okhulupirira Yehova akhazikika mtima

Nyimbo yokwerera.

1 Iwo akukhulupirira Yehova

akunga phiri laZiyoni, losasunthika, likhazikika kosatha.

2 Monga mapiri azingaYerusalemu,

momwemo Yehova azinga anthu ake,

kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.

3 Pakuti ndodo yachifumu ya choipa siidzapumula pa gawo la olungama;

kuti olungama asatulutse dzanja lao kuchita chosalungama.

4 Chitirani chokoma, Yehova, iwo okhala okoma;

iwo okhala oongoka mumtima mwao.

5 Koma iwo akupatula kutsata njira zao zokhotakhota,

Yehova adzawachotsa pamodzi ndi ochita zopanda pake.

Mtendere ukhale pa Israele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/125-eebef3497cf7bba78426c82c1869b5f7.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *