Okhulupirira Yehova akhazikika mtima
Nyimbo yokwerera.
1 Iwo akukhulupirira Yehova
akunga phiri laZiyoni, losasunthika, likhazikika kosatha.
2 Monga mapiri azingaYerusalemu,
momwemo Yehova azinga anthu ake,
kuyambira tsopano kufikira nthawi zonse.
3 Pakuti ndodo yachifumu ya choipa siidzapumula pa gawo la olungama;
kuti olungama asatulutse dzanja lao kuchita chosalungama.
4 Chitirani chokoma, Yehova, iwo okhala okoma;
iwo okhala oongoka mumtima mwao.
5 Koma iwo akupatula kutsata njira zao zokhotakhota,
Yehova adzawachotsa pamodzi ndi ochita zopanda pake.
Mtendere ukhale pa Israele.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/125-eebef3497cf7bba78426c82c1869b5f7.mp3?version_id=1068—