Pemphero lakuti akhululukidwe
Nyimbo yokwerera.
1 M’mozamamo ndinakufuulirani, Yehova.
2 Ambuye, imvani liu langa;
makutu anu akhale chimverere
mau a kupemba kwanga.
3 Mukasunga mphulupulu, Yehova,
adzakhala chilili ndani, Ambuye?
4 Koma kwa Inu kuli chikhululukiro,
kuti akuopeni.
5 Ndilindira Yehova, moyo wanga ulindira,
ndiyembekeza mau ake.
6 Moyo wanga uyang’anira Ambuye,
koposa alonda matanda kucha;
inde koposa alonda matanda kucha.
7 Israele, uyembekezere Yehova;
chifukwa kwa Yehova kuli chifundo,
kwaonso kuchulukira chiombolo.
8 Ndipo adzaombola Israele
ku mphulupulu zake zonse.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/130-08ede17c17095cb89fbacd5a4d727f95.mp3?version_id=1068—