Chikondano cha abale ndi chokoma
Nyimbo yokwerera; ya Davide.
1 Onani, nkokoma ndi kokondweretsa ndithu
kuti abale akhale pamodzi!
2 Ndiko ngati mafuta a mtengo wake pamutu,
akutsikira kundevu,
inde kundevu za Aroni;
akutsikira kumkawo wa zovala zake.
3 Ngati mame a ku Heremoni,
akutsikira pa mapiri aZiyoni.
Pakuti pamenepo Yehova analamulira dalitsolo,
ndilo moyo womka muyaya.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/133-de1654ae8ff13fcab0f2dd7436667ef5.mp3?version_id=1068—