Categories
MASALIMO

MASALIMO 135

Mulungu alemekezedwa pa ukulu wake. Mafano ndi achabe

1 Aleluya; Lemekezani dzina la Yehova!

Lemekezani inu atumiki a Yehova.

2 Inu akuimirira m’nyumba ya Yehova,

m’mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

3 Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino;

muimbire zolemekeza dzina lake; pakuti nkokondweretsa kutero.

4 Pakuti Yehova anadzisankhira Yakobo,

Israele, akhale chuma chake chenicheni.

5 Pakuti ndidziwa kuti Yehova ndi wamkulu,

ndi Ambuye wathu aposa milungu yonse.

6 Chilichonse chimkonda Yehova achichita,

kumwamba ndi padziko lapansi, m’nyanja ndi mozama monse.

7 Akweza mitambo ichokere ku malekezero a dziko lapansi;

ang’animitsa mphezi zidzetse mvula;

atulutsa mphepo mosungira mwake.

8 Anapanda oyamba a Ejipito,

kuyambira munthu kufikira zoweta.

9 Anatumiza zizindikiro ndi zodabwitsa pakati pako, Ejipito iwe,

paFaraondi pa omtumikira onse.

10 Ndiye amene anapandaamitunduambiri,

napha mafumu amphamvu;

11 Sihoni mfumu ya Aamori,

ndi Ogi mfumu ya Basani,

ndi maufumu onse a Kanani:

12 Ndipo anapereka dziko lao likhale cholowa,

cholowa cha kwa Israele anthu ake.

13 Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha;

chikumbukiro chanu, Yehova, kufikira mibadwomibadwo.

14 Pakuti Yehova adzaweruza anthu ake,

koma adzaleka atumiki ake.

15 Mafano a amitundu ndiwosilivandi golide,

ntchito ya manja a anthu.

16 Pakamwa ali napo koma osalankhula;

maso ali nao, koma osapenya;

17 makutu ali nao, koma osamva;

inde, pakamwa pao palibe mpweya.

18 Akuwapanga adzafanana nao;

inde, onse akuwakhulupirira.

19 A nyumba ya Israele inu, lemekezani Yehova:

A nyumba ya Aroni inu, lemekezani Yehova:

20 A nyumba ya Levi inu, lemekezani Yehova:

Inu akuopa Yehova, lemekezani Yehova.

21 Alemekezedwe Yehova kuchokera muZiyoni,

amene akhala muYerusalemu.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/135-17e07ebb8041dcceaa116f59e06f9179.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *