Mulungu alemekezedwa pa ukulu wake. Mafano ndi achabe
1 Aleluya; Lemekezani dzina la Yehova!
Lemekezani inu atumiki a Yehova.
2 Inu akuimirira m’nyumba ya Yehova,
m’mabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.
3 Lemekezani Yehova; pakuti Yehova ndiye wabwino;
muimbire zolemekeza dzina lake; pakuti nkokondweretsa kutero.
4 Pakuti Yehova anadzisankhira Yakobo,
Israele, akhale chuma chake chenicheni.
5 Pakuti ndidziwa kuti Yehova ndi wamkulu,
ndi Ambuye wathu aposa milungu yonse.
6 Chilichonse chimkonda Yehova achichita,
kumwamba ndi padziko lapansi, m’nyanja ndi mozama monse.
7 Akweza mitambo ichokere ku malekezero a dziko lapansi;
ang’animitsa mphezi zidzetse mvula;
atulutsa mphepo mosungira mwake.
8 Anapanda oyamba a Ejipito,
kuyambira munthu kufikira zoweta.
9 Anatumiza zizindikiro ndi zodabwitsa pakati pako, Ejipito iwe,
paFaraondi pa omtumikira onse.
10 Ndiye amene anapandaamitunduambiri,
napha mafumu amphamvu;
11 Sihoni mfumu ya Aamori,
ndi Ogi mfumu ya Basani,
ndi maufumu onse a Kanani:
12 Ndipo anapereka dziko lao likhale cholowa,
cholowa cha kwa Israele anthu ake.
13 Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha;
chikumbukiro chanu, Yehova, kufikira mibadwomibadwo.
14 Pakuti Yehova adzaweruza anthu ake,
koma adzaleka atumiki ake.
15 Mafano a amitundu ndiwosilivandi golide,
ntchito ya manja a anthu.
16 Pakamwa ali napo koma osalankhula;
maso ali nao, koma osapenya;
17 makutu ali nao, koma osamva;
inde, pakamwa pao palibe mpweya.
18 Akuwapanga adzafanana nao;
inde, onse akuwakhulupirira.
19 A nyumba ya Israele inu, lemekezani Yehova:
A nyumba ya Aroni inu, lemekezani Yehova:
20 A nyumba ya Levi inu, lemekezani Yehova:
Inu akuopa Yehova, lemekezani Yehova.
21 Alemekezedwe Yehova kuchokera muZiyoni,
amene akhala muYerusalemu.
Aleluya.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/135-17e07ebb8041dcceaa116f59e06f9179.mp3?version_id=1068—