Mulungu alemekezedwe pa chifundo chake
1 Yamikani Yehova pakuti ndiye wabwino;
pakuti chifundo chake nchosatha.
2 Yamikani Mulungu wa milungu;
pakuti chifundo chake nchosatha.
3 Yamikani Mbuye wa ambuye;
pakuti chifundo chake nchosatha.
4 Amene yekha achita zodabwitsa zazikulu;
pakuti chifundo chake nchosatha.
5 Amene analenga zakumwamba mwanzeru;
pakuti chifundo chake nchosatha.
6 Amene anayala dziko lapansi pamwamba pamadzi;
pakuti chifundo chake nchosatha.
7 Amene analenga miuni yaikulu;
pakuti chifundo chake nchosatha.
8 Dzuwa liweruze usana;
pakuti chifundo chake nchosatha.
9 Mwezi ndi nyenyezi ziweruze usiku;
pakuti chifundo chake nchosatha.
10 Iye amene anapandira Aejipito ana ao oyamba;
pakuti chifundo chake nchosatha.
11 Natulutsa Israele pakati pao;
pakuti chifundo chake nchosatha.
12 Ndi dzanja lamphamvu, ndi mkono wotambasuka;
pakuti chifundo chake nchosatha.
13 Amene anagawa magawo Nyanja Yofiira;
pakuti chifundo chake nchosatha.
14 Napititsa Israele pakati pake;
pakuti chifundo chake nchosatha.
15 NakhuthulaFaraondi khamu lake mu Nyanja Yofiira:
pakuti chifundo chake nchosatha.
16 Amene anatsogolera anthu ake m’chipululu;
pakuti chifundo chake nchosatha.
17 Amene anapanda mafumu aakulu;
pakuti chifundo chake nchosatha.
18 Ndipo anawapha mafumu omveka;
pakuti chifundo chake nchosatha.
19 Sihoni mfumu ya Aamori;
pakuti chifundo chake nchosatha.
20 Ndi Ogi mfumu ya Basani;
pakuti chifundo chake nchosatha.
21 Ndipo anapereka dziko lao likhale cholowa;
pakuti chifundo chake nchosatha.
22 Cholowa cha kwa Israele mtumiki wake;
pakuti chifundo chake nchosatha.
23 Amene anatikumbukira popepuka ife;
pakuti chifundo chake nchosatha.
24 Natikwatula kwa otisautsa;
pakuti chifundo chake nchosatha.
25 Ndiye wakupatsa nyama zonse chakudya;
pakuti chifundo chake nchosatha.
26 Yamikani Mulungu wa Kumwamba,
pakuti chifundo chake nchosatha.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/136-3ce0d50841b7431da42362b695c5d946.mp3?version_id=1068—