Categories
MASALIMO

MASALIMO 137

Kudandaula kwa Ayuda ku Babiloni

1 Ku mitsinje ya ku Babiloni,

kumeneko tinakhala pansi, inde tinalira,

pokumbukiraZiyoni.

2 Pa msondodzi uli m’mwemo

tinapachika mazeze athu.

3 Popeza pamenepo akutigwirawo anatifunsa nyimbo

ndipo akutizunza anafuna tisekere,

ndi kuti, Mutiimbire nyimbo imodzi ya ku Ziyoni.

4 Tidati, Tidzaimba bwanji nyimbo ya Yehova

m’dziko lachilendo?

5 Ndikakuiwalani, Yerusalemu,

dzanja lamanja langa liiwale luso lake.

6 Lilime langa limamatike kunsaya zanga,

ndikapanda kukumbukira inu;

ndikapanda kusankha Yerusalemu

koposa chimwemwe changa chopambana.

7 Yehova, kumbukirani ana a Edomu

tsiku la Yerusalemu;

amene adati, Gamulani, gamulani,

kufikira maziko ake.

8 Mwana wamkazi wa ku Babiloni,

iwe amene udzapasulidwa;

wodala iye amene adzakubwezera chilango

monga umo unatichitira ife.

9 Wodala iye amene adzagwira makanda ako,

ndi kuwaphwanya pathanthwe.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/137-ebdfdfe95ab47203bfc2919fabb5e2db.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *