Kudandaula kwa Ayuda ku Babiloni
1 Ku mitsinje ya ku Babiloni,
kumeneko tinakhala pansi, inde tinalira,
pokumbukiraZiyoni.
2 Pa msondodzi uli m’mwemo
tinapachika mazeze athu.
3 Popeza pamenepo akutigwirawo anatifunsa nyimbo
ndipo akutizunza anafuna tisekere,
ndi kuti, Mutiimbire nyimbo imodzi ya ku Ziyoni.
4 Tidati, Tidzaimba bwanji nyimbo ya Yehova
m’dziko lachilendo?
5 Ndikakuiwalani, Yerusalemu,
dzanja lamanja langa liiwale luso lake.
6 Lilime langa limamatike kunsaya zanga,
ndikapanda kukumbukira inu;
ndikapanda kusankha Yerusalemu
koposa chimwemwe changa chopambana.
7 Yehova, kumbukirani ana a Edomu
tsiku la Yerusalemu;
amene adati, Gamulani, gamulani,
kufikira maziko ake.
8 Mwana wamkazi wa ku Babiloni,
iwe amene udzapasulidwa;
wodala iye amene adzakubwezera chilango
monga umo unatichitira ife.
9 Wodala iye amene adzagwira makanda ako,
ndi kuwaphwanya pathanthwe.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/137-ebdfdfe95ab47203bfc2919fabb5e2db.mp3?version_id=1068—