Davide ayamika Mulungu pa kukhulupirika kwake, naneneratu kuti mafumu onse adzatero
Salimo la Davide.
1 Ndidzakuyamikani ndi mtima wanga wonse;
ndidzaimba zakukulemekezani patsogolo pa milungu.
2 Ndidzagwadira kuloza ku Kachisi wanu woyera,
ndi kuyamika dzina lanu,
chifukwa cha chifundo chanu ndi choonadi chanu;
popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.
3 Tsiku loitana ine, munandiyankha,
munandilimbitsa ndi mphamvu m’moyo mwanga.
4 Mafumu onse a padziko lapansi adzakuyamikani,
Yehova, popeza adamva mau a pakamwa panu.
5 Ndipo adzaimbira njira za Yehova;
pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukulu.
6 Angakhale Yehova ngwokwezeka, apenyanso wopepukayo;
koma wodzikuza amdziwira kutali.
7 Ndingakhale ndiyenda pakati pa nsautso, mudzandipatsa moyo;
mudzatambasula dzanja lanu pa mkwiyo wa adani anu,
ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.
8 Yehova adzanditsirizira za kwa ine:
Chifundo chanu, Yehova, chifikira kunthawi zonse:
Musasiye ntchito za manja anu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/138-baf99d1c1610bf2b5dde57b52d513be1.mp3?version_id=1068—