Categories
MASALIMO

MASALIMO 148

Zolengedwa zonse zilemekeze Mulungu

1 Aleluya.

Lemekezani Yehova kochokera kumwamba;

mlemekezeni m’misanje.

2 Mlemekezeni,angeloake onse;

mlemekezeni, makamu ake onse.

3 Mlemekezeni, dzuwa ndi mwezi;

mlemekezeni, nyenyezi zonse zounikira.

4 Mlemekezeni, m’mwambamwamba,

ndi madzi inu, a pamwamba pa thambo.

5 Alemekeze dzina la Yehova;

popeza analamulira, ndipo zinalengedwa.

6 Anazikhazikanso kunthawi za nthawi;

anazipatsa chilamulo chosatumphika.

7 Lemekezani Yehova kochokera ku dziko lapansi,

zinsomba inu, ndi malo ozama onse;

8 moto ndi matalala, chipale chofewa ndi nkhungu;

mphepo ya namondwe, yakuchita mau ake;

9 mapiri ndi zitunda zonse;

mitengo yazipatso ndi yamikungudza yonse:

10 Nyama zakuthengo ndi zoweta zonse;

zokwawa, ndi mbalame zakuuluka.

11 Mafumu a padziko ndi mitundu yonse ya anthu;

zinduna ndi oweruza onse a padziko.

12 Anyamata ndiponso anamwali;

okalamba pamodzi ndi ana.

13 Alemekeze dzina la Yehova;

pakuti dzina lake lokha ndi lokwezeka;

ulemerero wake uli pamwamba padziko lapansi ndi thambo.

14 Ndipo anakweza nyanga ya anthu ake,

chilemekezo cha okondedwa ake onse;

ndiwo ana a Israele, anthu a pafupi pa Iye.

Aleluya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/148-c66f417a2811e794129a4da622dd16f6.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *