Categories
MIYAMBO

MIYAMBO 13

1 Mwana wanzeru amamvera mwambo wa atate;

koma wonyoza samvera chidzudzulo.

2 Munthu adzadya zabwino ndi zipatso za m’kamwa mwake;

koma moyo wa achiwembu udzadya chiwawa.

3 Wogwira pakamwa pake asunga moyo wake;

koma woyasamula milomo yake adzaonongeka.

4 Moyo wa waulesi ukhumba osalandira kanthu;

koma moyo wa akhama udzalemera.

5 Wolungama ada mau onama;

koma woipa anyansa, nadzichititsa manyazi.

6 Chilungamo chitchinjiriza woongoka m’njira;

koma udyo ugwetsa wochimwa.

7 Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu;

alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi chuma chambiri.

8 Chiombolo cha moyo wa munthu ndicho chuma chake;

koma wosauka samva chidzudzulo.

9 Kuunika kwa olungama kukondwa;

koma nyali ya oipa idzazima.

10 Kudzikuza kupikisanitsa;

koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.

11 Chuma cholandiridwa mokangaza chidzachepa;

koma wokundika ndi dzanja adzaona zochuluka.

12 Chiyembekezo chozengereza chidwalitsa mtima;

koma pakufika chifunirocho ndicho mtengo wa moyo.

13 Wonyoza mau adziononga yekha;

koma woopa malangizo adzalandira mphotho.

14 Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,

apatutsa kumisampha ya imfa.

15 Nzeru yabwino ipatsa chisomo;

koma njira ya achiwembu ili makolokoto.

16 Yense wochenjera amachita mwanzeru;

koma wopusa aonetsa utsiru.

17 Mthenga wolakwa umagwa m’zoipa;

koma mtumiki wokhulupirika alamitsa.

18 Wokana mwambo adzasauka nanyozedwa;

koma wolabadira chidzudzulo adzalemekezedwa.

19 Chifuniro chikondweretsa moyo chitachitidwa;

koma kusiya zoipa kunyansa opusa.

20 Ukayenda ndi anzeru udzakhala wanzeru:

koma mnzao wa opusa adzaphwetekedwa.

21 Zoipa zilondola ochimwa;

koma olungama adzalandira mphotho yabwino.

22 Wabwino asiyira zidzukulu zake cholowa chabwino;

koma wochimwa angosungira wolungama chuma chake.

23 M’kulima kwa osauka muli zakudya zambiri;

koma zinazo zimaonongeka posowa chiweruzo.

24 Wolekerera mwanake osammenya amuda;

koma womkonda amyambize kumlanga.

25 Wolungama adya nakhutitsa moyo wake;

koma mimba ya oipa idzasowa.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/13-7e0058e913f39c50a46da6638a98fbd4.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *