1 Mkazi yense wanzeru amanga banja lake;
koma wopusa alipasula ndi manja ake.
2 Woyenda moongoka mtima aopa Yehova;
koma wokhota m’njira yake amnyoza.
3 M’kamwa mwa chitsiru muli nthyole ya kudzikuza;
koma milomo ya anzeru idzawasunga.
4 Popanda zoweta modyera muti see;
koma mphamvu ya ng’ombe ichulukitsa phindu.
5 Mboni yokhulupirika siidzanama;
koma mboni yonyenga imalankhula zonama.
6 Wonyoza afunafuna nzeru osaipeza;
koma wozindikira saona vuto m’kuphunzira.
7 Pita pamaso pa munthu wopusa,
sudzazindikira milomo yakudziwa.
8 Nzeru ya wochenjera ndiyo yakuti azindikire njira yake;
koma utsiru wa opusa ndiwo chinyengo.
9 Zitsiru zinyoza kupalamula;
koma mwa oongoka mtima muli chiyanjano.
10 Mtima udziwa kuwawa kwakekwake;
mlendo sadudukira ndi chimwemwe chake.
11 Nyumba ya oipa idzapasuka;
koma hema wa oongoka mtima adzakula.
12 Ilipo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka;
koma matsiriziro ake ndi njira za imfa.
13 Ngakhale m’kuseka mtima uwawa;
ndipo matsiriziro a chiphwete ndi chisoni.
14 Wobwerera m’mbuyo m’mtima adzakhuta njira yake;
koma munthu wabwino adzakhuta za mwa iye yekha.
15 Wachibwana akhulupirira mau onse;
koma wochenjera asamalira mayendedwe ake.
16 Wanzeru amaopa nasiya zoipa;
koma wopusa amanyada osatekeseka.
17 Wokangaza kukwiya adzachita utsiru;
ndipo munthu wa ziwembu adzadedwa.
18 Achibwana amalandira cholowa cha utsiru;
koma ochenjera amavala nzeru ngati korona.
19 Oipa amagwadira abwino,
ndi ochimwa pa makomo a olungama.
20 Waumphawi adedwa ndi anzake omwe;
koma akukonda wolemera achuluka.
21 Wonyoza anzake achimwa;
koma wochitira osauka chifundo adala.
22 Kodi oganizira zoipa sasochera?
Koma akuganizira zabwino adzalandira chifundo ndi ntheradi.
23 M’ntchito zonse muli phindu;
koma kulankhulalankhula kungopatsa umphawi.
24 Korona wa anzeru ndi chuma chao;
utsiru wa opusa ndiwo utsiru.
25 Mboni yoona imalanditsa miyoyo;
koma wolankhula zonama angonyenga.
26 Wakuopa Yehova akhulupirira kolimba;
ndipo ana ake adzakhala ndi pothawirapo.
27 Kuopa Yehova ndiko kasupe wa moyo,
kupatutsa kumisampha ya imfa.
28 Mu unyinji wa anthu muli ulemu wa mfumu;
koma popanda anthu kalonga aonongeka.
29 Wosakwiya msanga apambana kumvetsa;
koma wansontho akuza utsiru.
30 Mtima wabwino ndi moyo wa thupi;
koma nsanje ivunditsa mafupa.
31 Wotsendereza aumphawi atonza Mlengi wake;
koma wochitira wosauka chifundo amlemekeza.
32 Wochimwa adzakankhidwa m’kuipa kwake;
koma wolungama akhulupirirabe pomwalira.
33 Nzeru ikhalabe m’mtima wa wozindikira,
nidziwika pakati pa opusa.
34 Chilungamo chikuza mtundu wa anthu;
koma tchimo lichititsa fuko manyazi.
35 Mfumu ikomera mtima kapolo wochita mwanzeru;
koma idzakwiyira wochititsa manyazi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/14-9edb0598af40259cf8f0a0a5776b6b60.mp3?version_id=1068—