1 Wopanduka afunafuna chifuniro chake,
nakangana ndi nzeru yonse yeniyeni.
2 Wopusa sakondwera ndi kuzindikira;
koma kungovumbulutsa za m’mtima mwake.
3 Pakudza wamphulupulu padzanso kunyoza;
manyazi natsagana ndi chitonzo.
4 Mau a m’kamwa mwa munthu ndiwo madzi akuya;
kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wodzala.
5 Kukometsa mlandu wa wamphulupulu mwatsankho sikuli kwabwino,
ngakhale kuchitira chetera wolungama.
6 Milomo ya wopusa ifikitsa makangano;
ndipo m’kamwa mwake muputa kukwapulidwa.
7 M’kamwa mwa wopusa mumuononga,
milomo yake ikhala msampha wa moyo wake.
8 Mau akazitape akunga zakudya zolongosoka,
zotsikira m’kati mwa mimba.
9 Wogwira ntchito mwaulesi
ndiye mbale wake wa wosakaza.
10 Dzina la Yehova ndilo nsanja yolimba;
wolungama athamangiramo napulumuka.
11 Chuma cha wolemera ndicho mzinda wake wolimba;
alingalira kuti ndicho khoma lalitali.
12 Mtima wa munthu unyada asanaonongeke;
koma chifatso chitsogolera ulemu.
13 Wobwezera mau asanamvetse apusa,
nadzichititsa manyazi.
14 Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;
koma ndani angatukule mtima wosweka?
15 Mtima wa wozindikira umaphunzira;
khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.
16 Mtulo wa munthu umtsegulira njira,
numfikitsa pamaso pa akulu.
17 Woyamba kudzinenera ayang’anika wolungama;
koma mnzake afika namuululitsa zake zonse.
18 Maere aletsa makangano,
nulekanitsa amphamvu.
19 Kupembedza mbale utamchimwira nkovuta,
kulanda mzinda wolimba nkosavuta;
makangano akunga mipiringidzo ya linga.
20 Mimba ya munthu idzakhuta zipatso za m’kamwa mwake;
iye nadzakhuta phindu la milomo yake.
21 Lilime lili ndi mphamvu pa imfa ndi moyo;
wolikonda adzadya zipatso zake.
22 Wopeza mkazi apeza chinthu chabwino;
Yehova amkomera mtima.
23 Wosauka amadandaulira;
koma wolemera ayankha mwaukali.
24 Woyanjana ndi ambiri angodziononga;
koma lilipo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PRO/18-2ffd527be5c96b42d81c856660161173.mp3?version_id=1068—