Okoma ndi oipa amamva zomwezo. Khalani nazo zakupatsa Mulungu mokondwera
1 Pakuti zonsezi ndinazisunga mumtima ndikalondoletu zonsezi; kuti olungama ndi anzeru ndi ntchito zao ali m’manja a Mulungu; ngakhale kukonda ngakhale kudana anthu sadziwa; zonse zili m’tsogolo mwao.
2 Zonse zigwera onse chimodzimodzi; kanthu kamodzi kangogwera wolungama ndi woipa; ngakhale wabwino ndi woyera ndi wodetsedwa; ngakhale wopereka nsembe ndi wosapereka konse; wabwino alingana ndi wochimwa; wolumbira ndi woopa lumbira.
3 Ichi ndi choipa m’zonse zichitidwa pansi pano, chakuti kanthu kamodzi kagwera onse; indetu, mtimanso wa ana a anthu wadzala udyo, ndipo misala ili m’mtima wao akali ndi moyo, ndi pamenepo apita kwa akufa.
4 Pakuti woyang’ana ndi amoyo onse ali nacho chiyembekezo; pakuti galu wamoyo aposa mkango wakufa.
5 Pakuti amoyo adziwa kuti tidzafa; koma akufa sadziwa kanthu bii, sadzalandira mphotho; pakuti angoiwalika.
6 Chikondi chao ndi mdano wao ndi dumbo lao lomwe zatha tsopano; ndipo nthawi yamuyaya sagawa konse kanthu kalikonse kachitidwe pansi pano.
7 Tiye, idya zakudya zako mokondwa, numwe vinyo wako mosekera mtima; pakuti Mulungu wavomerezeratu zochita zako.
8 Zovala zako zikhale zoyera masiku onse; mutu wako usasowe mafuta.
9 Khalani mokondwa ndi mkazi umkonda masiku onse a moyo wako wachabe, umene Mulungu wakupatsa pansi pano masiku ako onse achabe; pakuti ilo ndi gawo lako la m’moyo ndi m’ntchito zimene uvutika nazo pansi pano.
10 Chilichonse dzanja lako lichipeza kuchichita, uchichite ndi mphamvu yako; pakuti mulibe ntchito ngakhale kulingirira ngakhale kudziwa, ngakhale nzeru, kumanda ulikupitako.
Nzeru ya mwini ilanditsa ena
11 Ndinabweranso ndi kuzindikira pansi pano kuti omwe athamanga msanga sapambana m’liwiro, ngakhale olimba sapambana m’nkhondo, ngakhale anzeru sapeza zakudya, ngakhale ozindikira bwino salemera, ngakhale odziwitsa sawakomera mtima; koma yense angoona zomgwera m’nthawi mwake.
12 Pakuti munthu sadziwatu mphindi yake; monga nsomba zigwidwa mu ukonde woipa, ndi mbalame zikodwa mumsampha, momwemo ana a anthu amagwidwa ndi nthawi ya tsoka, ngati msampha umene uwagwera modzidzimuka.
13 Ndaonanso nzeru pansi pano motero, ndipo inandionekera yaikulu;
14 panali mzinda waung’ono muli anthu owerengeka; ndipo inadzako mfumu yaikulu, nawuzinga ndi nkhondo, nkumanga malinga aakulu;
15 koma anapezedwamo mwamuna wanzeru wosauka, yemweyo napulumutsa mzindawo ndi nzeru yake; koma panalibe anthu anakumbukira wosauka ameneyo.
16 Pamenepo ndinati, Nzeru ipambana mphamvu; koma anyoza nzeru ya wosauka, osamvera mau ake.
17 Mau a anzeru achete amveka koposa kufuula kwa wolamulira mwa zitsiru.
18 Nzeru ipambana zida za nkhondo; koma wochimwa mmodzi aononga zabwino zambiri.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ECC/9-1c8c49bdff765158ebbeffe8acb88cf4.mp3?version_id=1068—