Categories
YESAYA

YESAYA 2

Ulemerero wa Israele m’tsogolomo, maweruzo a Mulungu pakatipo

1 Mau amene Yesaya mwana wa Amozi anaona, onena za Yuda ndiYerusalemu.

2 Ndipo padzakhala masiku otsiriza, kuti phiri la nyumba ya Yehova lidzakhazikika pansonga ya mapiri, ndipo lidzakwezedwa pamwamba pa zitunda; mitundu yonse idzasonkhana kumeneko.

3 Ndipo anthu ambiri adzanka, nati, Tiyeni tikwere kunka kuphiri la Yehova, kunyumba ya Mulungu wa Yakobo; ndipo Iye adzatiphunzitsa za njira zake, ndipo tidzayenda m’mayendedwe ake; chifukwa muZiyonimudzatuluka chilamulo, ndi mau a Yehova kuchokera mu Yerusalemu.

4 Iye adzaweruza pakati pa akunja, adzadzudzula mitundu yambiri ya anthu; ndipo iwo adzasula malupanga ao akhale zolimira, ndi nthungo zao zikhale makasu; mtundu sudzanyamula lupanga kumenyana ndi mtundu wina, ndipo sadzaphunziranso nkhondo.

5 Inu a nyumba ya Yakobo, tiyeni, tiyende m’kuwala kwa Yehova.

6 Chifukwa inu mwasiya anthu anu a nyumba ya Yakobo, chifukwa kuti iwo adzazidwa ndi miyambo ya kum’mawa, ndipo ali olaula ngati Afilisti, naomba m’manja ndi ana a achilendo.

7 Dziko lao ladzalasilivandi golide, ngakhale chuma chao nchosawerengeka; dziko lao lidzalanso akavalo, ngakhale magaleta ao ngosawerengeka.

8 Dziko lao ladzalanso mafano; iwo apembedza ntchito ya manja aoao, imene zala zaozao zinaipanga.

9 Munthu wachabe agwada pansi, ndi munthu wamkulu adzichepetsa, koma musawakhululukire.

10 Lowa m’phanga, bisala m’fumbi, kuchokera pa kuopsa kwa Yehova, ndi pa ulemerero wachifumu wake.

11 Maso a munthu akuyang’anira kumwamba adzatsitsidwa, ndi kudzikweza kwa anthu kudzaweramitsidwa pansi; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.

12 Chifukwa padzakhala tsiku la Yehova wa makamu pa zonse zonyada ndi zakudzikuza, ndi pa zonse zotukulidwa; ndipo zidzatsitsidwa;

13 ndi pa mitengo yonse yamkungudza ya Lebanoni, yaitali ndi yotukulidwa, ndi pa mitengo yonse yathundu ya Basani;

14 ndi pa mapiri onse aatali, ndi pa zitunda zonse zotukulidwa;

15 ndi pa nsanja zazitali zonse, ndi pa machemba onse;

16 ndi pa ngalawa zonse za Tarisisi, ndi pa zithunzithunzi zonse zokondweretsa.

17 Ndipo kudzikweza kwa munthu kudzaweramitsidwa pansi, kudzikuza kwa munthu kudzatsitsidwa; ndipo Yehova yekha adzakwezedwa tsiku limenelo.

18 Ndimo mafano adzapita psiti.

19 Anthu adzalowa m’mapanga a m’matanthwe, ndi m’maenje apansi, kuthawa kuopsa kwa Yehova, ndi ulemerero wachifumu wake, podzuka Iye kugwedeza dziko ndi mphamvu.

20 Tsiku limenelo munthu adzataya kumfuko ndi kumileme mafano ake asiliva ndi agolide amene anthu anampangira iye awapembedze;

21 kuti akalowe m’mapanga a m’matanthwe, ndi m’mindala a m’miyala, kuthawa kuopsa kwa Yehova, ndi ulemerero wachifumu wake, podzuka Iye kugwedeza dziko ndi mphamvu.

22 Siyani munthu, amene mpweya wake uli m’mphuno mwake; chifukwa m’mene awerengedwamo ndi muti?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/2-2584f1fca3e4a88a7624287f709bc971.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *