Categories
YESAYA

YESAYA 10

1 Tsoka kwa iwo amene alamulira malamulo osalungama, ndi kwa alembi olemba mphulupulu;

2 kuwapatulira osowa kuchiweruziro, ndi kuchotsera anthu anga aumphawi zoyenera zao, kuti alande za akazi amasiye, nafunkhire ana amasiye!

3 Ndipo mudzachita chiyani tsiku lakudza woyang’anira, ndi chipasuko chochokera kutali? Mudzathawira kwa yani kufuna kuthangatidwa? Mudzasiya kuti ulemerero wanu?

4 Adzangoweramira pansi pa andende, ndipo adzagwa pansi pa ophedwa. Mwa izi zonse mkwiyo wake sunachoke, koma dzanja lake lili chitambasulire.

Aneneratu za kuonongeka kwa Asiriya

5 Iwe Asiriya chibonga cha mkwiyo wanga, ndodo m’dzanja lake muli ukali wanga!

6 Ine ndidzamtumiza kumenyana ndi mtundu wosalemekeza, ndi pa anthu a mkwiyo wanga ndidzamlangiza, kuti afunkhe, agwire zolanda, awapondereze pansi, monga dothi la pamakwalala.

7 Koma iye safuna chotero, ndipo mtima wake suganizira chotero, koma mtima wake ulikufuna kusakaza, ndi kuduladula amitundu osawerengeka.

8 Popeza ati, Akalonga anga kodi sali onse mafumu?

9 Kodi Kalino sali wonga ngati Karikemisi? Kodi Hamati sali ngati Aripadi? Kodi Samariya sali ngati Damasiko?

10 Popeza dzanja langa lapeza maufumu a mafano, mafano ao osema anapambana ndi iwo a kuYerusalemundi ku Samariya;

11 monga ndachitira Samariya ndi mafano ake, momwemo kodi sindidzachitira Yerusalemu ndi mafano ake?

12 Chifukwa chake padzaoneka, kuti pamene Ambuye atatha ntchito yake yonse paphiri laZiyonindi pa Yerusalemu, ndidzalanga zipatso za mtima wolimba wa mfumu ya Asiriya, ndi ulemerero wa maso ake okwezedwa.

13 Popeza anati, Mwa mphamvu ya dzanja langa ndachita ichi, ndi mwa nzeru yanga; pakuti ine ndili wochenjera; ndachotsa malekezero a anthu, ndalanda chuma chao, ndagwetsa monga munthu wolimba mtima iwo okhala pa mipando yachifumu;

14 dzanja langa lapeza monga chisa, chuma cha mitundu ya anthu, ndipo monga munthu asonkhanitsa mazira osiyidwa, ine ndasonkhanitsa dziko lonse lapansi, ndipo panalibe chogwedeza phiko, kapena chotsegula pakamwa, kapena cholira pyepye.

15 Kodi nkhwangwa idzadzikweza yokha, pa iye amene adula nayo? Kodi chochekera chidzadzikweza chokha pa iye amene achigwedeza, ngati chibonga ingamgwedeze iye amene ainyamula, ngati ndodo inganyamule kanthu popeza ili mtengo.

16 Chifukwa chake Ambuye, Yehova wa makamu, adzatumiza kuonda mwa onenepa ake; ndipo pansi pa ulemerero wake padzayaka kutentha, konga ngati kutentha kwa moto.

17 Ndipo kuwala kwa Israele kudzakhala moto, ndi Woyera wake adzakhala lawi; ndipo lidzatentha ndi kuthetsa minga yake ndi lunguzi wake tsiku limodzi.

18 Ndipo adzanyeketsa ulemerero wa m’nkhalango yake, ndi wa m’munda wake wopatsa bwino, moyo ndi thupi; ndipo padzakhala monga ngati pokomoka wonyamula mbendera.

19 Ndipo mitengo yotsala ya m’nkhalango yake idzakhala yowerengeka, kuti mwana ailembera.

20 Ndipo padzakhala tsiku lomwelo, kuti otsala a Israele, ndi iwo amene anapulumuka a nyumba ya Yakobo, sadzatsamiranso iye amene anawamenya; koma adzatsamira Yehova Woyera wa Israele, ntheradi.

21 Otsala adzabwera, otsala a Yakobo, kwa Mulungu wamphamvu.

22 Popeza ngakhale anthu anu Israele akunga mchenga wa kunyanja, otsala ao okhaokha adzabwera; chionongeko chatsimikizidwa chilungamo chake chisefukira.

23 Pakuti Ambuye, Yehova wa makamu adzachita chionongeko chotsimikizidwa pakati padziko lonse lapansi.

24 Chifukwa chake atero Ambuye, Yehova wa makamu, Inu anthu anga okhala mu Ziyoni, musaope Asiriya; ngakhale amenya inu ndi chibonga, kapena kukusamulira iwe ndodo yake, monga amachitira Ejipito.

25 Pakuti patsala kamphindi, ndipo ukali udzathedwa ndi mkwiyo wanga wakuwaononga.

26 Ndipo Yehova wa makamu adzamuutsira chikoti, monga m’kuphedwa kwa Midiyani pa thanthwe la Orebu; ndipo chibonga chake chidzakhala pamwamba pa nyanja, ndipo adzaisamula monga anachitira Ejipito,

27 Ndipo padzakhala tsiku lomwelo, kuti katundu wake adzachoka pa phewa lako, ndi goli lake pakhosi pako; ndipo goli lidzathedwa chifukwa cha kudzoza mafuta.

28 Wafika ku Ayati, wapitirira kunka ku Migironi; pa Mikimasi asunga akatundu ake;

29 wapita pampata; wagona pa Geba, Rama anthunthumira; Gibea wa Saulo wathawa.

30 Fuula ndi mau ako iwe mwana wamkazi wa Galimu! Tamva, iwe Laisa! Iwe Anatoti wosauka!

31 Madimena ali wothawathawa; okhala mu Gebimu asonkhana kuti athawe.

32 Lero lomwe adzaima pa Nobu; agwedezera dzanja lake paphiri la mwana wamkazi wa Ziyoni, phiri la Yerusalemu.

33 Taonani, Ambuye Yehova wa makamu adzasadza nthambi moopsa; ndipo zazitali msinkhu zidzadulidwa, ndipo zazitali zidzagwetsedwa.

34 Ndipo adzadula nkhalango za m’thengo ndi chitsulo, ndipo Lebanoni adzagwa ndi wamphamvu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/10-1c274a3620c5390f1d8a0b5966e6ca5d.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *